Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Sura: Al-Hâqqah   Versetto:

Al-Hâqqah

ٱلۡحَآقَّةُ
Chakudza cha choonadi (chomwe ndi Qiyâma).
Esegesi in lingua araba:
مَا ٱلۡحَآقَّةُ
Kodi chakudza cha choonadi nchiyani?
Esegesi in lingua araba:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡحَآقَّةُ
Nanga nchiyani chikudziwitse za chakudza cha choonadicho?
Esegesi in lingua araba:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ وَعَادُۢ بِٱلۡقَارِعَةِ
Asamudu ndi Âdi adatsutsa zakudza kwa Qiyâma (yomwe idzadzidzimutsa zolengedwa mwamphamvu ndi zoopsa zake).
Esegesi in lingua araba:
فَأَمَّا ثَمُودُ فَأُهۡلِكُواْ بِٱلطَّاغِيَةِ
Tsono Asamudu adaonongedwa ndi phokoso lopyola muyeso, (lamphamvu kwambiri).
Esegesi in lingua araba:
وَأَمَّا عَادٞ فَأُهۡلِكُواْ بِرِيحٖ صَرۡصَرٍ عَاتِيَةٖ
Ndipo Âdi adaonongedwa ndi chimphepo cha mkuntho, chozizira, champhamvu kwambiri.
Esegesi in lingua araba:
سَخَّرَهَا عَلَيۡهِمۡ سَبۡعَ لَيَالٖ وَثَمَٰنِيَةَ أَيَّامٍ حُسُومٗاۖ فَتَرَى ٱلۡقَوۡمَ فِيهَا صَرۡعَىٰ كَأَنَّهُمۡ أَعۡجَازُ نَخۡلٍ خَاوِيَةٖ
Allah adachitumiza kwa iwo pa usiku usanu ndi uwiri ndi masana asanu ndi atatu mosadukiza; kotero ukadawaona ali lambalamba mmenemo ngati mathunthu a mitengo ya kanjedza yopanda kanthu m’kati mwake.
Esegesi in lingua araba:
فَهَلۡ تَرَىٰ لَهُم مِّنۢ بَاقِيَةٖ
Kodi nanga ukumuona wotsala mwa iwo?
Esegesi in lingua araba:
وَجَآءَ فِرۡعَوۡنُ وَمَن قَبۡلَهُۥ وَٱلۡمُؤۡتَفِكَٰتُ بِٱلۡخَاطِئَةِ
Ndipo Firiaun ndi amene adalipo iye asadabadwe, ndi khamu la anthu amidzi yotembenuzidwa (anthu a Luti) adadza ndi machimo (akulu).
Esegesi in lingua araba:
فَعَصَوۡاْ رَسُولَ رَبِّهِمۡ فَأَخَذَهُمۡ أَخۡذَةٗ رَّابِيَةً
Ndipo (yense wa iwowa) adanyoza Mtumiki wa Mbuye wawo; choncho adawalanga chilango chopitilira muyeso.
Esegesi in lingua araba:
إِنَّا لَمَّا طَغَا ٱلۡمَآءُ حَمَلۡنَٰكُمۡ فِي ٱلۡجَارِيَةِ
Ndithu pamene madzi adasefukira mopyola muyeso (mpaka kumeza mapiri nthawi ya chigumula cha Nowa) Ife tidakukwezani mchombo choyandama ndi kuyenda.
Esegesi in lingua araba:
لِنَجۡعَلَهَا لَكُمۡ تَذۡكِرَةٗ وَتَعِيَهَآ أُذُنٞ وَٰعِيَةٞ
Kuti tichichite (chochitikacho chomwe okhulupirira adapulumuka nacho; osakhulupirira adaonongeka nacho) kukhala lingaliro ndi phunziro kwa inu, ndikuti lisunge (nkhaniyi) khutu losunga.
Esegesi in lingua araba:
فَإِذَا نُفِخَ فِي ٱلصُّورِ نَفۡخَةٞ وَٰحِدَةٞ
Choncho likadzaimbidwa lipenga, kuimba kumodzi kokha (zamoyo zonse zidzafa).
Esegesi in lingua araba:
وَحُمِلَتِ ٱلۡأَرۡضُ وَٱلۡجِبَالُ فَدُكَّتَا دَكَّةٗ وَٰحِدَةٗ
Ndipo nthaka ndi mapiri nkuchotsedwa m’malo mwake ndi kuphwanyidwa kamodzi nkamodzi.
Esegesi in lingua araba:
فَيَوۡمَئِذٖ وَقَعَتِ ٱلۡوَاقِعَةُ
Chomwecho tsiku limenelo, chochitika chidzachitika (imene ili Qiyâma).
Esegesi in lingua araba:
وَٱنشَقَّتِ ٱلسَّمَآءُ فَهِيَ يَوۡمَئِذٖ وَاهِيَةٞ
Ndipo thambo lidzasweka choncho ilo tsiku limenelo lidzakhala lofooka (pamene lidali lolimba).
Esegesi in lingua araba:
وَٱلۡمَلَكُ عَلَىٰٓ أَرۡجَآئِهَاۚ وَيَحۡمِلُ عَرۡشَ رَبِّكَ فَوۡقَهُمۡ يَوۡمَئِذٖ ثَمَٰنِيَةٞ
Ndipo angelo adzakhala m’mphepete mwake, ndipo pamwamba pawo tsiku limenero (angelo) asanu ndi atatu adzasenza Arsh (Mpando wachifumu) ya Mbuye wako.
Esegesi in lingua araba:
يَوۡمَئِذٖ تُعۡرَضُونَ لَا تَخۡفَىٰ مِنكُمۡ خَافِيَةٞ
Tsiku limenelo mudzabweretsedwa ku chiweruzo; sichidzabisika chilichonse chobisika mwa inu.
Esegesi in lingua araba:
فَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ بِيَمِينِهِۦ فَيَقُولُ هَآؤُمُ ٱقۡرَءُواْ كِتَٰبِيَهۡ
Tsono amene adzapatsidwa kaundula wake chakudzanja lakumanja kwake adzanena (mokondwa kwa amene ali m’phepete mwake): “Tengani! Werengani kaundula wanga!”
Esegesi in lingua araba:
إِنِّي ظَنَنتُ أَنِّي مُلَٰقٍ حِسَابِيَهۡ
“Ndithudi ine ndidatsimikiza (pa dziko lapansi) kuti ndidzakumana ndi chiwerengero changa.”
Esegesi in lingua araba:
فَهُوَ فِي عِيشَةٖ رَّاضِيَةٖ
Choncho, iye adzakhala m’moyo wosangalatsa.
Esegesi in lingua araba:
فِي جَنَّةٍ عَالِيَةٖ
M’munda wapamwamba.
Esegesi in lingua araba:
قُطُوفُهَا دَانِيَةٞ
Zipatso zake zoyandikira pansi (zosavuta kuzithyola).
Esegesi in lingua araba:
كُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ هَنِيٓـَٔۢا بِمَآ أَسۡلَفۡتُمۡ فِي ٱلۡأَيَّامِ ٱلۡخَالِيَةِ
(Adzawauza kuti:) “Idyani, ndipo imwani mosangalala pa zimene mudatsogoza mmasiku aja adapita (a pa dziko lapansi).”
Esegesi in lingua araba:
وَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ بِشِمَالِهِۦ فَيَقُولُ يَٰلَيۡتَنِي لَمۡ أُوتَ كِتَٰبِيَهۡ
Ndipo amene adzapatsidwe kaundula wake kudzanja lake lamanzere, adzanena (modandaula): “Kalanga ine! Ndiponi ndikadapanda kupatsidwa kaundula wangayu!”
Esegesi in lingua araba:
وَلَمۡ أَدۡرِ مَا حِسَابِيَهۡ
“Nkusadziwa chiwerengero changa!”
Esegesi in lingua araba:
يَٰلَيۡتَهَا كَانَتِ ٱلۡقَاضِيَةَ
“Ha! imfa ija ikadandimaliziratu (ndi kundilekanitsa ine ndi zimenezi).”
Esegesi in lingua araba:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنِّي مَالِيَهۡۜ
“Chuma changa sichidandithandize!”
Esegesi in lingua araba:
هَلَكَ عَنِّي سُلۡطَٰنِيَهۡ
“Mphamvu zanga (ndi moyo wanga wathanzi) zandichokera!”
Esegesi in lingua araba:
خُذُوهُ فَغُلُّوهُ
(Kudzanenedwa kwa angelo oyang’anira Jahena): Mgwireni ndipo mnjateni (pomphatikiza manja ndi khosi)!
Esegesi in lingua araba:
ثُمَّ ٱلۡجَحِيمَ صَلُّوهُ
Kenako mponyeni ku Moto.
Esegesi in lingua araba:
ثُمَّ فِي سِلۡسِلَةٖ ذَرۡعُهَا سَبۡعُونَ ذِرَاعٗا فَٱسۡلُكُوهُ
Kenakonso mulowetseni mtcheni lotalika mikwamba makumi asanu ndi awiri!
Esegesi in lingua araba:
إِنَّهُۥ كَانَ لَا يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndithudi, iye sadali kukhulupirira mwa Allah wamkulu.
Esegesi in lingua araba:
وَلَا يَحُضُّ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Sadalinso kulimbikitsa zodyetsa osauka.
Esegesi in lingua araba:
فَلَيۡسَ لَهُ ٱلۡيَوۡمَ هَٰهُنَا حَمِيمٞ
Basi, lero kuno alibe bwenzi (lomthandiza).
Esegesi in lingua araba:
وَلَا طَعَامٌ إِلَّا مِنۡ غِسۡلِينٖ
Ngakhale chakudya kupatula mafinya (a anthu a ku Moto).
Esegesi in lingua araba:
لَّا يَأۡكُلُهُۥٓ إِلَّا ٱلۡخَٰطِـُٔونَ
Zomwe palibe angazidye kupatula ochimwa (mwadala).
Esegesi in lingua araba:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِمَا تُبۡصِرُونَ
Choncho ndikulumbilira zimene mukuziona.
Esegesi in lingua araba:
وَمَا لَا تُبۡصِرُونَ
Ndi zimene simukuziona.
Esegesi in lingua araba:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلُ رَسُولٖ كَرِيمٖ
Ndithudi iyi (Qur’an) ndiliwu la mthenga wolemekezeka (Jibril).
Esegesi in lingua araba:
وَمَا هُوَ بِقَوۡلِ شَاعِرٖۚ قَلِيلٗا مَّا تُؤۡمِنُونَ
Ndipo simawu a mlakatuli, ndi zochepa zimene mukuzikhulupirira.
Esegesi in lingua araba:
وَلَا بِقَوۡلِ كَاهِنٖۚ قَلِيلٗا مَّا تَذَكَّرُونَ
Ndiponso simawu a mlosi, ndizochepa zimene mmakumbukira!
Esegesi in lingua araba:
تَنزِيلٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
(Ichi ndi) chivumbulutso chochokera kwa Mbuye wa zolengedwa.
Esegesi in lingua araba:
وَلَوۡ تَقَوَّلَ عَلَيۡنَا بَعۡضَ ٱلۡأَقَاوِيلِ
Ndipo (Mneneri) akadatipekera bodza linalake.
Esegesi in lingua araba:
لَأَخَذۡنَا مِنۡهُ بِٱلۡيَمِينِ
Tikadamgwira (mwamphamvu) ndimkono wamanja.
Esegesi in lingua araba:
ثُمَّ لَقَطَعۡنَا مِنۡهُ ٱلۡوَتِينَ
Ndipo tikadadula mwa iye mtsempha wa moyo (kotero kuti ndikuferatu nthawi yomweyo).
Esegesi in lingua araba:
فَمَا مِنكُم مِّنۡ أَحَدٍ عَنۡهُ حَٰجِزِينَ
Sipakadapezeka aliyense mwa inu womteteza (kuchilango Chathu).
Esegesi in lingua araba:
وَإِنَّهُۥ لَتَذۡكِرَةٞ لِّلۡمُتَّقِينَ
Ndithu iyi (Qur’an) ndi phunziro labwino kwa owopa (Allah.)
Esegesi in lingua araba:
وَإِنَّا لَنَعۡلَمُ أَنَّ مِنكُم مُّكَذِّبِينَ
Ndithu Ife, tikudziwa kuti ena mwa inu ndiotsutsa (Qur’an).
Esegesi in lingua araba:
وَإِنَّهُۥ لَحَسۡرَةٌ عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo ndithu iyi (Qur’an) idzakhala chowadandaulitsa (chachikulu) osakhulupirira (pamene adzaona chilango chawo ndi mtendere wa okhulupirira).
Esegesi in lingua araba:
وَإِنَّهُۥ لَحَقُّ ٱلۡيَقِينِ
Ndithu iyoyi ndichoonadi Chotsimikizika; (mulibe chikaiko),
Esegesi in lingua araba:
فَسَبِّحۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلۡعَظِيمِ
Basi, lemekeza dzina la Mbuye wako Wamkulu (pitiriza kutamanda dzina Lake).
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Sura: Al-Hâqqah
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi