クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 章: 不可避な時章   節:

不可避な時章

ٱلۡحَآقَّةُ
Chakudza cha choonadi (chomwe ndi Qiyâma).
アラビア語 クルアーン注釈:
مَا ٱلۡحَآقَّةُ
Kodi chakudza cha choonadi nchiyani?
アラビア語 クルアーン注釈:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡحَآقَّةُ
Nanga nchiyani chikudziwitse za chakudza cha choonadicho?
アラビア語 クルアーン注釈:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ وَعَادُۢ بِٱلۡقَارِعَةِ
Asamudu ndi Âdi adatsutsa zakudza kwa Qiyâma (yomwe idzadzidzimutsa zolengedwa mwamphamvu ndi zoopsa zake).
アラビア語 クルアーン注釈:
فَأَمَّا ثَمُودُ فَأُهۡلِكُواْ بِٱلطَّاغِيَةِ
Tsono Asamudu adaonongedwa ndi phokoso lopyola muyeso, (lamphamvu kwambiri).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَأَمَّا عَادٞ فَأُهۡلِكُواْ بِرِيحٖ صَرۡصَرٍ عَاتِيَةٖ
Ndipo Âdi adaonongedwa ndi chimphepo cha mkuntho, chozizira, champhamvu kwambiri.
アラビア語 クルアーン注釈:
سَخَّرَهَا عَلَيۡهِمۡ سَبۡعَ لَيَالٖ وَثَمَٰنِيَةَ أَيَّامٍ حُسُومٗاۖ فَتَرَى ٱلۡقَوۡمَ فِيهَا صَرۡعَىٰ كَأَنَّهُمۡ أَعۡجَازُ نَخۡلٍ خَاوِيَةٖ
Allah adachitumiza kwa iwo pa usiku usanu ndi uwiri ndi masana asanu ndi atatu mosadukiza; kotero ukadawaona ali lambalamba mmenemo ngati mathunthu a mitengo ya kanjedza yopanda kanthu m’kati mwake.
アラビア語 クルアーン注釈:
فَهَلۡ تَرَىٰ لَهُم مِّنۢ بَاقِيَةٖ
Kodi nanga ukumuona wotsala mwa iwo?
アラビア語 クルアーン注釈:
وَجَآءَ فِرۡعَوۡنُ وَمَن قَبۡلَهُۥ وَٱلۡمُؤۡتَفِكَٰتُ بِٱلۡخَاطِئَةِ
Ndipo Firiaun ndi amene adalipo iye asadabadwe, ndi khamu la anthu amidzi yotembenuzidwa (anthu a Luti) adadza ndi machimo (akulu).
アラビア語 クルアーン注釈:
فَعَصَوۡاْ رَسُولَ رَبِّهِمۡ فَأَخَذَهُمۡ أَخۡذَةٗ رَّابِيَةً
Ndipo (yense wa iwowa) adanyoza Mtumiki wa Mbuye wawo; choncho adawalanga chilango chopitilira muyeso.
アラビア語 クルアーン注釈:
إِنَّا لَمَّا طَغَا ٱلۡمَآءُ حَمَلۡنَٰكُمۡ فِي ٱلۡجَارِيَةِ
Ndithu pamene madzi adasefukira mopyola muyeso (mpaka kumeza mapiri nthawi ya chigumula cha Nowa) Ife tidakukwezani mchombo choyandama ndi kuyenda.
アラビア語 クルアーン注釈:
لِنَجۡعَلَهَا لَكُمۡ تَذۡكِرَةٗ وَتَعِيَهَآ أُذُنٞ وَٰعِيَةٞ
Kuti tichichite (chochitikacho chomwe okhulupirira adapulumuka nacho; osakhulupirira adaonongeka nacho) kukhala lingaliro ndi phunziro kwa inu, ndikuti lisunge (nkhaniyi) khutu losunga.
アラビア語 クルアーン注釈:
فَإِذَا نُفِخَ فِي ٱلصُّورِ نَفۡخَةٞ وَٰحِدَةٞ
Choncho likadzaimbidwa lipenga, kuimba kumodzi kokha (zamoyo zonse zidzafa).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَحُمِلَتِ ٱلۡأَرۡضُ وَٱلۡجِبَالُ فَدُكَّتَا دَكَّةٗ وَٰحِدَةٗ
Ndipo nthaka ndi mapiri nkuchotsedwa m’malo mwake ndi kuphwanyidwa kamodzi nkamodzi.
アラビア語 クルアーン注釈:
فَيَوۡمَئِذٖ وَقَعَتِ ٱلۡوَاقِعَةُ
Chomwecho tsiku limenelo, chochitika chidzachitika (imene ili Qiyâma).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَٱنشَقَّتِ ٱلسَّمَآءُ فَهِيَ يَوۡمَئِذٖ وَاهِيَةٞ
Ndipo thambo lidzasweka choncho ilo tsiku limenelo lidzakhala lofooka (pamene lidali lolimba).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَٱلۡمَلَكُ عَلَىٰٓ أَرۡجَآئِهَاۚ وَيَحۡمِلُ عَرۡشَ رَبِّكَ فَوۡقَهُمۡ يَوۡمَئِذٖ ثَمَٰنِيَةٞ
Ndipo angelo adzakhala m’mphepete mwake, ndipo pamwamba pawo tsiku limenero (angelo) asanu ndi atatu adzasenza Arsh (Mpando wachifumu) ya Mbuye wako.
アラビア語 クルアーン注釈:
يَوۡمَئِذٖ تُعۡرَضُونَ لَا تَخۡفَىٰ مِنكُمۡ خَافِيَةٞ
Tsiku limenelo mudzabweretsedwa ku chiweruzo; sichidzabisika chilichonse chobisika mwa inu.
アラビア語 クルアーン注釈:
فَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ بِيَمِينِهِۦ فَيَقُولُ هَآؤُمُ ٱقۡرَءُواْ كِتَٰبِيَهۡ
Tsono amene adzapatsidwa kaundula wake chakudzanja lakumanja kwake adzanena (mokondwa kwa amene ali m’phepete mwake): “Tengani! Werengani kaundula wanga!”
アラビア語 クルアーン注釈:
إِنِّي ظَنَنتُ أَنِّي مُلَٰقٍ حِسَابِيَهۡ
“Ndithudi ine ndidatsimikiza (pa dziko lapansi) kuti ndidzakumana ndi chiwerengero changa.”
アラビア語 クルアーン注釈:
فَهُوَ فِي عِيشَةٖ رَّاضِيَةٖ
Choncho, iye adzakhala m’moyo wosangalatsa.
アラビア語 クルアーン注釈:
فِي جَنَّةٍ عَالِيَةٖ
M’munda wapamwamba.
アラビア語 クルアーン注釈:
قُطُوفُهَا دَانِيَةٞ
Zipatso zake zoyandikira pansi (zosavuta kuzithyola).
アラビア語 クルアーン注釈:
كُلُواْ وَٱشۡرَبُواْ هَنِيٓـَٔۢا بِمَآ أَسۡلَفۡتُمۡ فِي ٱلۡأَيَّامِ ٱلۡخَالِيَةِ
(Adzawauza kuti:) “Idyani, ndipo imwani mosangalala pa zimene mudatsogoza mmasiku aja adapita (a pa dziko lapansi).”
アラビア語 クルアーン注釈:
وَأَمَّا مَنۡ أُوتِيَ كِتَٰبَهُۥ بِشِمَالِهِۦ فَيَقُولُ يَٰلَيۡتَنِي لَمۡ أُوتَ كِتَٰبِيَهۡ
Ndipo amene adzapatsidwe kaundula wake kudzanja lake lamanzere, adzanena (modandaula): “Kalanga ine! Ndiponi ndikadapanda kupatsidwa kaundula wangayu!”
アラビア語 クルアーン注釈:
وَلَمۡ أَدۡرِ مَا حِسَابِيَهۡ
“Nkusadziwa chiwerengero changa!”
アラビア語 クルアーン注釈:
يَٰلَيۡتَهَا كَانَتِ ٱلۡقَاضِيَةَ
“Ha! imfa ija ikadandimaliziratu (ndi kundilekanitsa ine ndi zimenezi).”
アラビア語 クルアーン注釈:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنِّي مَالِيَهۡۜ
“Chuma changa sichidandithandize!”
アラビア語 クルアーン注釈:
هَلَكَ عَنِّي سُلۡطَٰنِيَهۡ
“Mphamvu zanga (ndi moyo wanga wathanzi) zandichokera!”
アラビア語 クルアーン注釈:
خُذُوهُ فَغُلُّوهُ
(Kudzanenedwa kwa angelo oyang’anira Jahena): Mgwireni ndipo mnjateni (pomphatikiza manja ndi khosi)!
アラビア語 クルアーン注釈:
ثُمَّ ٱلۡجَحِيمَ صَلُّوهُ
Kenako mponyeni ku Moto.
アラビア語 クルアーン注釈:
ثُمَّ فِي سِلۡسِلَةٖ ذَرۡعُهَا سَبۡعُونَ ذِرَاعٗا فَٱسۡلُكُوهُ
Kenakonso mulowetseni mtcheni lotalika mikwamba makumi asanu ndi awiri!
アラビア語 クルアーン注釈:
إِنَّهُۥ كَانَ لَا يُؤۡمِنُ بِٱللَّهِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndithudi, iye sadali kukhulupirira mwa Allah wamkulu.
アラビア語 クルアーン注釈:
وَلَا يَحُضُّ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Sadalinso kulimbikitsa zodyetsa osauka.
アラビア語 クルアーン注釈:
فَلَيۡسَ لَهُ ٱلۡيَوۡمَ هَٰهُنَا حَمِيمٞ
Basi, lero kuno alibe bwenzi (lomthandiza).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَلَا طَعَامٌ إِلَّا مِنۡ غِسۡلِينٖ
Ngakhale chakudya kupatula mafinya (a anthu a ku Moto).
アラビア語 クルアーン注釈:
لَّا يَأۡكُلُهُۥٓ إِلَّا ٱلۡخَٰطِـُٔونَ
Zomwe palibe angazidye kupatula ochimwa (mwadala).
アラビア語 クルアーン注釈:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِمَا تُبۡصِرُونَ
Choncho ndikulumbilira zimene mukuziona.
アラビア語 クルアーン注釈:
وَمَا لَا تُبۡصِرُونَ
Ndi zimene simukuziona.
アラビア語 クルアーン注釈:
إِنَّهُۥ لَقَوۡلُ رَسُولٖ كَرِيمٖ
Ndithudi iyi (Qur’an) ndiliwu la mthenga wolemekezeka (Jibril).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَمَا هُوَ بِقَوۡلِ شَاعِرٖۚ قَلِيلٗا مَّا تُؤۡمِنُونَ
Ndipo simawu a mlakatuli, ndi zochepa zimene mukuzikhulupirira.
アラビア語 クルアーン注釈:
وَلَا بِقَوۡلِ كَاهِنٖۚ قَلِيلٗا مَّا تَذَكَّرُونَ
Ndiponso simawu a mlosi, ndizochepa zimene mmakumbukira!
アラビア語 クルアーン注釈:
تَنزِيلٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
(Ichi ndi) chivumbulutso chochokera kwa Mbuye wa zolengedwa.
アラビア語 クルアーン注釈:
وَلَوۡ تَقَوَّلَ عَلَيۡنَا بَعۡضَ ٱلۡأَقَاوِيلِ
Ndipo (Mneneri) akadatipekera bodza linalake.
アラビア語 クルアーン注釈:
لَأَخَذۡنَا مِنۡهُ بِٱلۡيَمِينِ
Tikadamgwira (mwamphamvu) ndimkono wamanja.
アラビア語 クルアーン注釈:
ثُمَّ لَقَطَعۡنَا مِنۡهُ ٱلۡوَتِينَ
Ndipo tikadadula mwa iye mtsempha wa moyo (kotero kuti ndikuferatu nthawi yomweyo).
アラビア語 クルアーン注釈:
فَمَا مِنكُم مِّنۡ أَحَدٍ عَنۡهُ حَٰجِزِينَ
Sipakadapezeka aliyense mwa inu womteteza (kuchilango Chathu).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَإِنَّهُۥ لَتَذۡكِرَةٞ لِّلۡمُتَّقِينَ
Ndithu iyi (Qur’an) ndi phunziro labwino kwa owopa (Allah.)
アラビア語 クルアーン注釈:
وَإِنَّا لَنَعۡلَمُ أَنَّ مِنكُم مُّكَذِّبِينَ
Ndithu Ife, tikudziwa kuti ena mwa inu ndiotsutsa (Qur’an).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَإِنَّهُۥ لَحَسۡرَةٌ عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo ndithu iyi (Qur’an) idzakhala chowadandaulitsa (chachikulu) osakhulupirira (pamene adzaona chilango chawo ndi mtendere wa okhulupirira).
アラビア語 クルアーン注釈:
وَإِنَّهُۥ لَحَقُّ ٱلۡيَقِينِ
Ndithu iyoyi ndichoonadi Chotsimikizika; (mulibe chikaiko),
アラビア語 クルアーン注釈:
فَسَبِّحۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلۡعَظِيمِ
Basi, lemekeza dzina la Mbuye wako Wamkulu (pitiriza kutamanda dzina Lake).
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 章: 不可避な時章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる