Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Al-Moddassir (Iemand die Gebundeld is)   Vers:

Soerat Al-Moddassir (Iemand die Gebundeld is)

يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمُدَّثِّرُ
E iwe wadziphimba (nsalu)!
Arabische uitleg van de Qur'an:
قُمۡ فَأَنذِرۡ
Imilira ndipo uwachenjeze (anthu za chilango cha Allah).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَرَبَّكَ فَكَبِّرۡ
Ndipo Mbuye wako (Yekha) umkulitse (pomulemekeza).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَثِيَابَكَ فَطَهِّرۡ
Ndipo nsalu zako uziyeretse (ndi madzi ku uve).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلرُّجۡزَ فَٱهۡجُرۡ
Ndiponso zoipa (monga mafano ndi zina zonse ) zipewe.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَلَا تَمۡنُن تَسۡتَكۡثِرُ
Usapatse (anthu) ncholinga choti ulandire zambiri.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَلِرَبِّكَ فَٱصۡبِرۡ
Chifukwa cha Mbuye wako, pirira (ku malamulo Ake poleka zomwe waletsa ndi kuchita zimene walamula).
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَإِذَا نُقِرَ فِي ٱلنَّاقُورِ
Ndipo likadzaimbidwa lipenga,
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَذَٰلِكَ يَوۡمَئِذٖ يَوۡمٌ عَسِيرٌ
Tsiku limenelo lidzakhala tsiku lovuta.
Arabische uitleg van de Qur'an:
عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ غَيۡرُ يَسِيرٖ
Kwa osakhulupirira, silidzakhala lofewa.
Arabische uitleg van de Qur'an:
ذَرۡنِي وَمَنۡ خَلَقۡتُ وَحِيدٗا
Ndisiye ndiamene ndidamlenga Ndekha,
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَجَعَلۡتُ لَهُۥ مَالٗا مَّمۡدُودٗا
Ndipo ndampatsa chuma chambiri.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَبَنِينَ شُهُودٗا
Ndi ana okhala nawo (paliponse).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَمَهَّدتُّ لَهُۥ تَمۡهِيدٗا
Ndipo ndamkonzera (ulemelero), kumkonzera (kwabwino).
Arabische uitleg van de Qur'an:
ثُمَّ يَطۡمَعُ أَنۡ أَزِيدَ
Kenako ali ndi dyera kuti ndimuonjezere (zina popanda kuthokoza).
Arabische uitleg van de Qur'an:
كَلَّآۖ إِنَّهُۥ كَانَ لِأٓيَٰتِنَا عَنِيدٗا
Koma sichoncho! Ndithu iye adali kutsutsa zizindikiro Zathu.
Arabische uitleg van de Qur'an:
سَأُرۡهِقُهُۥ صَعُودًا
Ndidzamkakamiza kuchilango chovuta; (kukwera phiri la ku Moto limene sakatha kulikwera).
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِنَّهُۥ فَكَّرَ وَقَدَّرَ
Iye adalingalira (mu mtima mwake) ndi kukonza bwino (chonena chonyoza Qur’an).
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَقُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Choncho waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Arabische uitleg van de Qur'an:
ثُمَّ قُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Ndiponso waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Arabische uitleg van de Qur'an:
ثُمَّ نَظَرَ
Kenako adayang’anayang’ana (nkhope za anthu).
Arabische uitleg van de Qur'an:
ثُمَّ عَبَسَ وَبَسَرَ
Kenakonso adachita tsinya ndikukwinya nkhope (kwambiri ndi mkwiyo).
Arabische uitleg van de Qur'an:
ثُمَّ أَدۡبَرَ وَٱسۡتَكۡبَرَ
Kenakonso adanyoza choonadi ndi kudzikweza (posachivomereza),
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَقَالَ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ يُؤۡثَرُ
Adati: “Sichina ichi (Qur’an) koma ndi matsenga amene adalandiridwa (kuchokera kwa amatsenga akale),
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا قَوۡلُ ٱلۡبَشَرِ
Sichina ichi koma ndi mawu a anthu!”
Arabische uitleg van de Qur'an:
سَأُصۡلِيهِ سَقَرَ
Posachedwa ndimlowetsa ku ‘Saqara.’
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سَقَرُ
Nanga ndi chiyani chingakudziwitse za ‘Saqara?’
Arabische uitleg van de Qur'an:
لَا تُبۡقِي وَلَا تَذَرُ
(Ndi moto umene) siusiya (mnofu) ndiponso siusiya (fupa),
Arabische uitleg van de Qur'an:
لَوَّاحَةٞ لِّلۡبَشَرِ
Wopsereza ndi kudetsa khungu.
Arabische uitleg van de Qur'an:
عَلَيۡهَا تِسۡعَةَ عَشَرَ
Kumeneko kuli khumi ndi asanu ndi anayi (alonda oyang’anira Motowo.)
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَمَا جَعَلۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلنَّارِ إِلَّا مَلَٰٓئِكَةٗۖ وَمَا جَعَلۡنَا عِدَّتَهُمۡ إِلَّا فِتۡنَةٗ لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ لِيَسۡتَيۡقِنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَيَزۡدَادَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِيمَٰنٗا وَلَا يَرۡتَابَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَلِيَقُولَ ٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ وَٱلۡكَٰفِرُونَ مَاذَآ أَرَادَ ٱللَّهُ بِهَٰذَا مَثَلٗاۚ كَذَٰلِكَ يُضِلُّ ٱللَّهُ مَن يَشَآءُ وَيَهۡدِي مَن يَشَآءُۚ وَمَا يَعۡلَمُ جُنُودَ رَبِّكَ إِلَّا هُوَۚ وَمَا هِيَ إِلَّا ذِكۡرَىٰ لِلۡبَشَرِ
Ndipo sitidaike oyang’anira ku Moto (kukhala anthu) koma angelo; ndipo sitidaike chiwerengero chawo koma ndimayesero kwa amene sadakhulupirire, kuti atsimikize amene adapatsidwa mabuku (zimene Qur’an ikunena za chiwerengero cha angelo a ku Moto) ndiponso kuti chionjezeke chikhulupiliro kwa amene akhulupirira, ndikuti asapeneke amene adapatsidwa mabuku pamodzi ndi okhulupirira. Ndiponso kuti amene m’mitima mwawo muli matenda (matenda achinyengo) komanso osakhulupirira anene: “Kodi Allah akulinganji pa fanizo limeneli?” Momwemo Allah akumulekelera kusokera amene wamfuna, ndipo akumuongola amene wamfuna ndipo palibe amene angadziwe magulu a nkhondo a Mbuye wako kupatula Iye mwini. (Kutchula moto ndi zam’kati mwake) sichina koma ndichenjezo kwa anthu.
Arabische uitleg van de Qur'an:
كَلَّا وَٱلۡقَمَرِ
Sichoncho; ndikulumbilira mwezi,
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلَّيۡلِ إِذۡ أَدۡبَرَ
Ndi usiku pamene ukuchoka,
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَٱلصُّبۡحِ إِذَآ أَسۡفَرَ
Ndi m’bandakucha pamene kukuyera.
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِنَّهَا لَإِحۡدَى ٱلۡكُبَرِ
Ndithu uwo, (moto wa Jahannam) ndi chimodzi mwa malodza akulu,
Arabische uitleg van de Qur'an:
نَذِيرٗا لِّلۡبَشَرِ
Ndi chenjezo kwa anthu,
Arabische uitleg van de Qur'an:
لِمَن شَآءَ مِنكُمۡ أَن يَتَقَدَّمَ أَوۡ يَتَأَخَّرَ
Kwa yemwe wafuna mwa inu kutsogola (pochita zabwino zokamthandiza tsiku louka kwa akufa) kapena kutsalira (ndi za m’dziko).
Arabische uitleg van de Qur'an:
كُلُّ نَفۡسِۭ بِمَا كَسَبَتۡ رَهِينَةٌ
Mzimu uliwonse ukakhala chikole ndi zimene udachita.
Arabische uitleg van de Qur'an:
إِلَّآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡيَمِينِ
Kupatula akudzanja lamanja (Asilamu amene adadzimasula okha potembenukira kwa Allah).
Arabische uitleg van de Qur'an:
فِي جَنَّٰتٖ يَتَسَآءَلُونَ
(Iwo) adzakhala m’minda (yosasimbika kukongola kwake) akufunsana wina ndi mnzake,
Arabische uitleg van de Qur'an:
عَنِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Za anthu oipa,
Arabische uitleg van de Qur'an:
مَا سَلَكَكُمۡ فِي سَقَرَ
(Kuti): “Nchiyani chakulowetsani ku Moto?”
Arabische uitleg van de Qur'an:
قَالُواْ لَمۡ نَكُ مِنَ ٱلۡمُصَلِّينَ
Adzanena: “Sitidali m’gulu la omwe adali kupemphera (Swala).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَلَمۡ نَكُ نُطۡعِمُ ٱلۡمِسۡكِينَ
Ndiponso sitidali kuwadyetsa masikini.
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَكُنَّا نَخُوضُ مَعَ ٱلۡخَآئِضِينَ
Koma tinkangomira (m’zachabe ndi zabodza) pamodzi ndi omira (m’menemo).
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَكُنَّا نُكَذِّبُ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndiponso tidali kutsutsa za tsiku la malipiro.
Arabische uitleg van de Qur'an:
حَتَّىٰٓ أَتَىٰنَا ٱلۡيَقِينُ
Mpaka imfa idatifika.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَمَا تَنفَعُهُمۡ شَفَٰعَةُ ٱلشَّٰفِعِينَ
Choncho siwudzawathandiza uwomboli wa awomboli.
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَمَا لَهُمۡ عَنِ ٱلتَّذۡكِرَةِ مُعۡرِضِينَ
Kodi ali ndi chiyani iwo pakuti azinyozera chenjezoli (limene lili Qur’an?)
Arabische uitleg van de Qur'an:
كَأَنَّهُمۡ حُمُرٞ مُّسۡتَنفِرَةٞ
(Akuyenda mothamanga kuti asamve chenjezoli) ngati kuti iwo ndi mbidzi zothawa,
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَرَّتۡ مِن قَسۡوَرَةِۭ
(Zimene) zikuthawa mkango.
Arabische uitleg van de Qur'an:
بَلۡ يُرِيدُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُؤۡتَىٰ صُحُفٗا مُّنَشَّرَةٗ
Ati akufuna aliyense mwa iwo apatsidwe kalata zotambasulidwa (zimene zitsimikize uthenga wa Mneneri Muhammad{s.a.w}).
Arabische uitleg van de Qur'an:
كَلَّاۖ بَل لَّا يَخَافُونَ ٱلۡأٓخِرَةَ
Sichoncho! Koma kuti iwo sakuopa tsiku lachimaliziro.
Arabische uitleg van de Qur'an:
كَلَّآ إِنَّهُۥ تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithu ichi (Qur’an) ndichikumbutso (chokwanira).
Arabische uitleg van de Qur'an:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Choncho amene wafuna achikumbukire (amene sakufuna ndizake)!
Arabische uitleg van de Qur'an:
وَمَا يَذۡكُرُونَ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُۚ هُوَ أَهۡلُ ٱلتَّقۡوَىٰ وَأَهۡلُ ٱلۡمَغۡفِرَةِ
Ndipo sangakumbukire pokhapokha Allah atafuna. Iye ndiye Amene ali woyenera kumuopa, ndiponso ndiye Mwini kukhululukira (amene akumuopa).
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Surah: Soerat Al-Moddassir (Iemand die Gebundeld is)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit