Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Sourate: AL-MOUDDATHTHIR   Verset:

AL-MOUDDATHTHIR

يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمُدَّثِّرُ
E iwe wadziphimba (nsalu)!
Les exégèses en arabe:
قُمۡ فَأَنذِرۡ
Imilira ndipo uwachenjeze (anthu za chilango cha Allah).
Les exégèses en arabe:
وَرَبَّكَ فَكَبِّرۡ
Ndipo Mbuye wako (Yekha) umkulitse (pomulemekeza).
Les exégèses en arabe:
وَثِيَابَكَ فَطَهِّرۡ
Ndipo nsalu zako uziyeretse (ndi madzi ku uve).
Les exégèses en arabe:
وَٱلرُّجۡزَ فَٱهۡجُرۡ
Ndiponso zoipa (monga mafano ndi zina zonse ) zipewe.
Les exégèses en arabe:
وَلَا تَمۡنُن تَسۡتَكۡثِرُ
Usapatse (anthu) ncholinga choti ulandire zambiri.
Les exégèses en arabe:
وَلِرَبِّكَ فَٱصۡبِرۡ
Chifukwa cha Mbuye wako, pirira (ku malamulo Ake poleka zomwe waletsa ndi kuchita zimene walamula).
Les exégèses en arabe:
فَإِذَا نُقِرَ فِي ٱلنَّاقُورِ
Ndipo likadzaimbidwa lipenga,
Les exégèses en arabe:
فَذَٰلِكَ يَوۡمَئِذٖ يَوۡمٌ عَسِيرٌ
Tsiku limenelo lidzakhala tsiku lovuta.
Les exégèses en arabe:
عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ غَيۡرُ يَسِيرٖ
Kwa osakhulupirira, silidzakhala lofewa.
Les exégèses en arabe:
ذَرۡنِي وَمَنۡ خَلَقۡتُ وَحِيدٗا
Ndisiye ndiamene ndidamlenga Ndekha,
Les exégèses en arabe:
وَجَعَلۡتُ لَهُۥ مَالٗا مَّمۡدُودٗا
Ndipo ndampatsa chuma chambiri.
Les exégèses en arabe:
وَبَنِينَ شُهُودٗا
Ndi ana okhala nawo (paliponse).
Les exégèses en arabe:
وَمَهَّدتُّ لَهُۥ تَمۡهِيدٗا
Ndipo ndamkonzera (ulemelero), kumkonzera (kwabwino).
Les exégèses en arabe:
ثُمَّ يَطۡمَعُ أَنۡ أَزِيدَ
Kenako ali ndi dyera kuti ndimuonjezere (zina popanda kuthokoza).
Les exégèses en arabe:
كَلَّآۖ إِنَّهُۥ كَانَ لِأٓيَٰتِنَا عَنِيدٗا
Koma sichoncho! Ndithu iye adali kutsutsa zizindikiro Zathu.
Les exégèses en arabe:
سَأُرۡهِقُهُۥ صَعُودًا
Ndidzamkakamiza kuchilango chovuta; (kukwera phiri la ku Moto limene sakatha kulikwera).
Les exégèses en arabe:
إِنَّهُۥ فَكَّرَ وَقَدَّرَ
Iye adalingalira (mu mtima mwake) ndi kukonza bwino (chonena chonyoza Qur’an).
Les exégèses en arabe:
فَقُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Choncho waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Les exégèses en arabe:
ثُمَّ قُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Ndiponso waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Les exégèses en arabe:
ثُمَّ نَظَرَ
Kenako adayang’anayang’ana (nkhope za anthu).
Les exégèses en arabe:
ثُمَّ عَبَسَ وَبَسَرَ
Kenakonso adachita tsinya ndikukwinya nkhope (kwambiri ndi mkwiyo).
Les exégèses en arabe:
ثُمَّ أَدۡبَرَ وَٱسۡتَكۡبَرَ
Kenakonso adanyoza choonadi ndi kudzikweza (posachivomereza),
Les exégèses en arabe:
فَقَالَ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ يُؤۡثَرُ
Adati: “Sichina ichi (Qur’an) koma ndi matsenga amene adalandiridwa (kuchokera kwa amatsenga akale),
Les exégèses en arabe:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا قَوۡلُ ٱلۡبَشَرِ
Sichina ichi koma ndi mawu a anthu!”
Les exégèses en arabe:
سَأُصۡلِيهِ سَقَرَ
Posachedwa ndimlowetsa ku ‘Saqara.’
Les exégèses en arabe:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سَقَرُ
Nanga ndi chiyani chingakudziwitse za ‘Saqara?’
Les exégèses en arabe:
لَا تُبۡقِي وَلَا تَذَرُ
(Ndi moto umene) siusiya (mnofu) ndiponso siusiya (fupa),
Les exégèses en arabe:
لَوَّاحَةٞ لِّلۡبَشَرِ
Wopsereza ndi kudetsa khungu.
Les exégèses en arabe:
عَلَيۡهَا تِسۡعَةَ عَشَرَ
Kumeneko kuli khumi ndi asanu ndi anayi (alonda oyang’anira Motowo.)
Les exégèses en arabe:
وَمَا جَعَلۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلنَّارِ إِلَّا مَلَٰٓئِكَةٗۖ وَمَا جَعَلۡنَا عِدَّتَهُمۡ إِلَّا فِتۡنَةٗ لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ لِيَسۡتَيۡقِنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَيَزۡدَادَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِيمَٰنٗا وَلَا يَرۡتَابَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَلِيَقُولَ ٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ وَٱلۡكَٰفِرُونَ مَاذَآ أَرَادَ ٱللَّهُ بِهَٰذَا مَثَلٗاۚ كَذَٰلِكَ يُضِلُّ ٱللَّهُ مَن يَشَآءُ وَيَهۡدِي مَن يَشَآءُۚ وَمَا يَعۡلَمُ جُنُودَ رَبِّكَ إِلَّا هُوَۚ وَمَا هِيَ إِلَّا ذِكۡرَىٰ لِلۡبَشَرِ
Ndipo sitidaike oyang’anira ku Moto (kukhala anthu) koma angelo; ndipo sitidaike chiwerengero chawo koma ndimayesero kwa amene sadakhulupirire, kuti atsimikize amene adapatsidwa mabuku (zimene Qur’an ikunena za chiwerengero cha angelo a ku Moto) ndiponso kuti chionjezeke chikhulupiliro kwa amene akhulupirira, ndikuti asapeneke amene adapatsidwa mabuku pamodzi ndi okhulupirira. Ndiponso kuti amene m’mitima mwawo muli matenda (matenda achinyengo) komanso osakhulupirira anene: “Kodi Allah akulinganji pa fanizo limeneli?” Momwemo Allah akumulekelera kusokera amene wamfuna, ndipo akumuongola amene wamfuna ndipo palibe amene angadziwe magulu a nkhondo a Mbuye wako kupatula Iye mwini. (Kutchula moto ndi zam’kati mwake) sichina koma ndichenjezo kwa anthu.
Les exégèses en arabe:
كَلَّا وَٱلۡقَمَرِ
Sichoncho; ndikulumbilira mwezi,
Les exégèses en arabe:
وَٱلَّيۡلِ إِذۡ أَدۡبَرَ
Ndi usiku pamene ukuchoka,
Les exégèses en arabe:
وَٱلصُّبۡحِ إِذَآ أَسۡفَرَ
Ndi m’bandakucha pamene kukuyera.
Les exégèses en arabe:
إِنَّهَا لَإِحۡدَى ٱلۡكُبَرِ
Ndithu uwo, (moto wa Jahannam) ndi chimodzi mwa malodza akulu,
Les exégèses en arabe:
نَذِيرٗا لِّلۡبَشَرِ
Ndi chenjezo kwa anthu,
Les exégèses en arabe:
لِمَن شَآءَ مِنكُمۡ أَن يَتَقَدَّمَ أَوۡ يَتَأَخَّرَ
Kwa yemwe wafuna mwa inu kutsogola (pochita zabwino zokamthandiza tsiku louka kwa akufa) kapena kutsalira (ndi za m’dziko).
Les exégèses en arabe:
كُلُّ نَفۡسِۭ بِمَا كَسَبَتۡ رَهِينَةٌ
Mzimu uliwonse ukakhala chikole ndi zimene udachita.
Les exégèses en arabe:
إِلَّآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡيَمِينِ
Kupatula akudzanja lamanja (Asilamu amene adadzimasula okha potembenukira kwa Allah).
Les exégèses en arabe:
فِي جَنَّٰتٖ يَتَسَآءَلُونَ
(Iwo) adzakhala m’minda (yosasimbika kukongola kwake) akufunsana wina ndi mnzake,
Les exégèses en arabe:
عَنِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Za anthu oipa,
Les exégèses en arabe:
مَا سَلَكَكُمۡ فِي سَقَرَ
(Kuti): “Nchiyani chakulowetsani ku Moto?”
Les exégèses en arabe:
قَالُواْ لَمۡ نَكُ مِنَ ٱلۡمُصَلِّينَ
Adzanena: “Sitidali m’gulu la omwe adali kupemphera (Swala).
Les exégèses en arabe:
وَلَمۡ نَكُ نُطۡعِمُ ٱلۡمِسۡكِينَ
Ndiponso sitidali kuwadyetsa masikini.
Les exégèses en arabe:
وَكُنَّا نَخُوضُ مَعَ ٱلۡخَآئِضِينَ
Koma tinkangomira (m’zachabe ndi zabodza) pamodzi ndi omira (m’menemo).
Les exégèses en arabe:
وَكُنَّا نُكَذِّبُ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndiponso tidali kutsutsa za tsiku la malipiro.
Les exégèses en arabe:
حَتَّىٰٓ أَتَىٰنَا ٱلۡيَقِينُ
Mpaka imfa idatifika.”
Les exégèses en arabe:
فَمَا تَنفَعُهُمۡ شَفَٰعَةُ ٱلشَّٰفِعِينَ
Choncho siwudzawathandiza uwomboli wa awomboli.
Les exégèses en arabe:
فَمَا لَهُمۡ عَنِ ٱلتَّذۡكِرَةِ مُعۡرِضِينَ
Kodi ali ndi chiyani iwo pakuti azinyozera chenjezoli (limene lili Qur’an?)
Les exégèses en arabe:
كَأَنَّهُمۡ حُمُرٞ مُّسۡتَنفِرَةٞ
(Akuyenda mothamanga kuti asamve chenjezoli) ngati kuti iwo ndi mbidzi zothawa,
Les exégèses en arabe:
فَرَّتۡ مِن قَسۡوَرَةِۭ
(Zimene) zikuthawa mkango.
Les exégèses en arabe:
بَلۡ يُرِيدُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُؤۡتَىٰ صُحُفٗا مُّنَشَّرَةٗ
Ati akufuna aliyense mwa iwo apatsidwe kalata zotambasulidwa (zimene zitsimikize uthenga wa Mneneri Muhammad{s.a.w}).
Les exégèses en arabe:
كَلَّاۖ بَل لَّا يَخَافُونَ ٱلۡأٓخِرَةَ
Sichoncho! Koma kuti iwo sakuopa tsiku lachimaliziro.
Les exégèses en arabe:
كَلَّآ إِنَّهُۥ تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithu ichi (Qur’an) ndichikumbutso (chokwanira).
Les exégèses en arabe:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Choncho amene wafuna achikumbukire (amene sakufuna ndizake)!
Les exégèses en arabe:
وَمَا يَذۡكُرُونَ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُۚ هُوَ أَهۡلُ ٱلتَّقۡوَىٰ وَأَهۡلُ ٱلۡمَغۡفِرَةِ
Ndipo sangakumbukire pokhapokha Allah atafuna. Iye ndiye Amene ali woyenera kumuopa, ndiponso ndiye Mwini kukhululukira (amene akumuopa).
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Sourate: AL-MOUDDATHTHIR
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture