Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu El Mudethir   Ajeti:

Suretu El Mudethir

يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمُدَّثِّرُ
E iwe wadziphimba (nsalu)!
Tefsiret në gjuhën arabe:
قُمۡ فَأَنذِرۡ
Imilira ndipo uwachenjeze (anthu za chilango cha Allah).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَرَبَّكَ فَكَبِّرۡ
Ndipo Mbuye wako (Yekha) umkulitse (pomulemekeza).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَثِيَابَكَ فَطَهِّرۡ
Ndipo nsalu zako uziyeretse (ndi madzi ku uve).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلرُّجۡزَ فَٱهۡجُرۡ
Ndiponso zoipa (monga mafano ndi zina zonse ) zipewe.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَلَا تَمۡنُن تَسۡتَكۡثِرُ
Usapatse (anthu) ncholinga choti ulandire zambiri.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَلِرَبِّكَ فَٱصۡبِرۡ
Chifukwa cha Mbuye wako, pirira (ku malamulo Ake poleka zomwe waletsa ndi kuchita zimene walamula).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَإِذَا نُقِرَ فِي ٱلنَّاقُورِ
Ndipo likadzaimbidwa lipenga,
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَذَٰلِكَ يَوۡمَئِذٖ يَوۡمٌ عَسِيرٌ
Tsiku limenelo lidzakhala tsiku lovuta.
Tefsiret në gjuhën arabe:
عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ غَيۡرُ يَسِيرٖ
Kwa osakhulupirira, silidzakhala lofewa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
ذَرۡنِي وَمَنۡ خَلَقۡتُ وَحِيدٗا
Ndisiye ndiamene ndidamlenga Ndekha,
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَجَعَلۡتُ لَهُۥ مَالٗا مَّمۡدُودٗا
Ndipo ndampatsa chuma chambiri.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَبَنِينَ شُهُودٗا
Ndi ana okhala nawo (paliponse).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَهَّدتُّ لَهُۥ تَمۡهِيدٗا
Ndipo ndamkonzera (ulemelero), kumkonzera (kwabwino).
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ يَطۡمَعُ أَنۡ أَزِيدَ
Kenako ali ndi dyera kuti ndimuonjezere (zina popanda kuthokoza).
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّآۖ إِنَّهُۥ كَانَ لِأٓيَٰتِنَا عَنِيدٗا
Koma sichoncho! Ndithu iye adali kutsutsa zizindikiro Zathu.
Tefsiret në gjuhën arabe:
سَأُرۡهِقُهُۥ صَعُودًا
Ndidzamkakamiza kuchilango chovuta; (kukwera phiri la ku Moto limene sakatha kulikwera).
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّهُۥ فَكَّرَ وَقَدَّرَ
Iye adalingalira (mu mtima mwake) ndi kukonza bwino (chonena chonyoza Qur’an).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَقُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Choncho waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ قُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Ndiponso waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ نَظَرَ
Kenako adayang’anayang’ana (nkhope za anthu).
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ عَبَسَ وَبَسَرَ
Kenakonso adachita tsinya ndikukwinya nkhope (kwambiri ndi mkwiyo).
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ أَدۡبَرَ وَٱسۡتَكۡبَرَ
Kenakonso adanyoza choonadi ndi kudzikweza (posachivomereza),
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَقَالَ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ يُؤۡثَرُ
Adati: “Sichina ichi (Qur’an) koma ndi matsenga amene adalandiridwa (kuchokera kwa amatsenga akale),
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا قَوۡلُ ٱلۡبَشَرِ
Sichina ichi koma ndi mawu a anthu!”
Tefsiret në gjuhën arabe:
سَأُصۡلِيهِ سَقَرَ
Posachedwa ndimlowetsa ku ‘Saqara.’
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سَقَرُ
Nanga ndi chiyani chingakudziwitse za ‘Saqara?’
Tefsiret në gjuhën arabe:
لَا تُبۡقِي وَلَا تَذَرُ
(Ndi moto umene) siusiya (mnofu) ndiponso siusiya (fupa),
Tefsiret në gjuhën arabe:
لَوَّاحَةٞ لِّلۡبَشَرِ
Wopsereza ndi kudetsa khungu.
Tefsiret në gjuhën arabe:
عَلَيۡهَا تِسۡعَةَ عَشَرَ
Kumeneko kuli khumi ndi asanu ndi anayi (alonda oyang’anira Motowo.)
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَا جَعَلۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلنَّارِ إِلَّا مَلَٰٓئِكَةٗۖ وَمَا جَعَلۡنَا عِدَّتَهُمۡ إِلَّا فِتۡنَةٗ لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ لِيَسۡتَيۡقِنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَيَزۡدَادَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِيمَٰنٗا وَلَا يَرۡتَابَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَلِيَقُولَ ٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ وَٱلۡكَٰفِرُونَ مَاذَآ أَرَادَ ٱللَّهُ بِهَٰذَا مَثَلٗاۚ كَذَٰلِكَ يُضِلُّ ٱللَّهُ مَن يَشَآءُ وَيَهۡدِي مَن يَشَآءُۚ وَمَا يَعۡلَمُ جُنُودَ رَبِّكَ إِلَّا هُوَۚ وَمَا هِيَ إِلَّا ذِكۡرَىٰ لِلۡبَشَرِ
Ndipo sitidaike oyang’anira ku Moto (kukhala anthu) koma angelo; ndipo sitidaike chiwerengero chawo koma ndimayesero kwa amene sadakhulupirire, kuti atsimikize amene adapatsidwa mabuku (zimene Qur’an ikunena za chiwerengero cha angelo a ku Moto) ndiponso kuti chionjezeke chikhulupiliro kwa amene akhulupirira, ndikuti asapeneke amene adapatsidwa mabuku pamodzi ndi okhulupirira. Ndiponso kuti amene m’mitima mwawo muli matenda (matenda achinyengo) komanso osakhulupirira anene: “Kodi Allah akulinganji pa fanizo limeneli?” Momwemo Allah akumulekelera kusokera amene wamfuna, ndipo akumuongola amene wamfuna ndipo palibe amene angadziwe magulu a nkhondo a Mbuye wako kupatula Iye mwini. (Kutchula moto ndi zam’kati mwake) sichina koma ndichenjezo kwa anthu.
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّا وَٱلۡقَمَرِ
Sichoncho; ndikulumbilira mwezi,
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلَّيۡلِ إِذۡ أَدۡبَرَ
Ndi usiku pamene ukuchoka,
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلصُّبۡحِ إِذَآ أَسۡفَرَ
Ndi m’bandakucha pamene kukuyera.
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّهَا لَإِحۡدَى ٱلۡكُبَرِ
Ndithu uwo, (moto wa Jahannam) ndi chimodzi mwa malodza akulu,
Tefsiret në gjuhën arabe:
نَذِيرٗا لِّلۡبَشَرِ
Ndi chenjezo kwa anthu,
Tefsiret në gjuhën arabe:
لِمَن شَآءَ مِنكُمۡ أَن يَتَقَدَّمَ أَوۡ يَتَأَخَّرَ
Kwa yemwe wafuna mwa inu kutsogola (pochita zabwino zokamthandiza tsiku louka kwa akufa) kapena kutsalira (ndi za m’dziko).
Tefsiret në gjuhën arabe:
كُلُّ نَفۡسِۭ بِمَا كَسَبَتۡ رَهِينَةٌ
Mzimu uliwonse ukakhala chikole ndi zimene udachita.
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِلَّآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡيَمِينِ
Kupatula akudzanja lamanja (Asilamu amene adadzimasula okha potembenukira kwa Allah).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فِي جَنَّٰتٖ يَتَسَآءَلُونَ
(Iwo) adzakhala m’minda (yosasimbika kukongola kwake) akufunsana wina ndi mnzake,
Tefsiret në gjuhën arabe:
عَنِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Za anthu oipa,
Tefsiret në gjuhën arabe:
مَا سَلَكَكُمۡ فِي سَقَرَ
(Kuti): “Nchiyani chakulowetsani ku Moto?”
Tefsiret në gjuhën arabe:
قَالُواْ لَمۡ نَكُ مِنَ ٱلۡمُصَلِّينَ
Adzanena: “Sitidali m’gulu la omwe adali kupemphera (Swala).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَلَمۡ نَكُ نُطۡعِمُ ٱلۡمِسۡكِينَ
Ndiponso sitidali kuwadyetsa masikini.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَكُنَّا نَخُوضُ مَعَ ٱلۡخَآئِضِينَ
Koma tinkangomira (m’zachabe ndi zabodza) pamodzi ndi omira (m’menemo).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَكُنَّا نُكَذِّبُ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndiponso tidali kutsutsa za tsiku la malipiro.
Tefsiret në gjuhën arabe:
حَتَّىٰٓ أَتَىٰنَا ٱلۡيَقِينُ
Mpaka imfa idatifika.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَمَا تَنفَعُهُمۡ شَفَٰعَةُ ٱلشَّٰفِعِينَ
Choncho siwudzawathandiza uwomboli wa awomboli.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَمَا لَهُمۡ عَنِ ٱلتَّذۡكِرَةِ مُعۡرِضِينَ
Kodi ali ndi chiyani iwo pakuti azinyozera chenjezoli (limene lili Qur’an?)
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَأَنَّهُمۡ حُمُرٞ مُّسۡتَنفِرَةٞ
(Akuyenda mothamanga kuti asamve chenjezoli) ngati kuti iwo ndi mbidzi zothawa,
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَرَّتۡ مِن قَسۡوَرَةِۭ
(Zimene) zikuthawa mkango.
Tefsiret në gjuhën arabe:
بَلۡ يُرِيدُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُؤۡتَىٰ صُحُفٗا مُّنَشَّرَةٗ
Ati akufuna aliyense mwa iwo apatsidwe kalata zotambasulidwa (zimene zitsimikize uthenga wa Mneneri Muhammad{s.a.w}).
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّاۖ بَل لَّا يَخَافُونَ ٱلۡأٓخِرَةَ
Sichoncho! Koma kuti iwo sakuopa tsiku lachimaliziro.
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّآ إِنَّهُۥ تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithu ichi (Qur’an) ndichikumbutso (chokwanira).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Choncho amene wafuna achikumbukire (amene sakufuna ndizake)!
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَا يَذۡكُرُونَ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُۚ هُوَ أَهۡلُ ٱلتَّقۡوَىٰ وَأَهۡلُ ٱلۡمَغۡفِرَةِ
Ndipo sangakumbukire pokhapokha Allah atafuna. Iye ndiye Amene ali woyenera kumuopa, ndiponso ndiye Mwini kukhululukira (amene akumuopa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu El Mudethir
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll