Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا * - Mealler fihristi


Anlam tercümesi Sure: Sûretu'l-Muddessir   Ayet:

Sûretu'l-Muddessir

يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمُدَّثِّرُ
E iwe wadziphimba (nsalu)!
Arapça tefsirler:
قُمۡ فَأَنذِرۡ
Imilira ndipo uwachenjeze (anthu za chilango cha Allah).
Arapça tefsirler:
وَرَبَّكَ فَكَبِّرۡ
Ndipo Mbuye wako (Yekha) umkulitse (pomulemekeza).
Arapça tefsirler:
وَثِيَابَكَ فَطَهِّرۡ
Ndipo nsalu zako uziyeretse (ndi madzi ku uve).
Arapça tefsirler:
وَٱلرُّجۡزَ فَٱهۡجُرۡ
Ndiponso zoipa (monga mafano ndi zina zonse ) zipewe.
Arapça tefsirler:
وَلَا تَمۡنُن تَسۡتَكۡثِرُ
Usapatse (anthu) ncholinga choti ulandire zambiri.
Arapça tefsirler:
وَلِرَبِّكَ فَٱصۡبِرۡ
Chifukwa cha Mbuye wako, pirira (ku malamulo Ake poleka zomwe waletsa ndi kuchita zimene walamula).
Arapça tefsirler:
فَإِذَا نُقِرَ فِي ٱلنَّاقُورِ
Ndipo likadzaimbidwa lipenga,
Arapça tefsirler:
فَذَٰلِكَ يَوۡمَئِذٖ يَوۡمٌ عَسِيرٌ
Tsiku limenelo lidzakhala tsiku lovuta.
Arapça tefsirler:
عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ غَيۡرُ يَسِيرٖ
Kwa osakhulupirira, silidzakhala lofewa.
Arapça tefsirler:
ذَرۡنِي وَمَنۡ خَلَقۡتُ وَحِيدٗا
Ndisiye ndiamene ndidamlenga Ndekha,
Arapça tefsirler:
وَجَعَلۡتُ لَهُۥ مَالٗا مَّمۡدُودٗا
Ndipo ndampatsa chuma chambiri.
Arapça tefsirler:
وَبَنِينَ شُهُودٗا
Ndi ana okhala nawo (paliponse).
Arapça tefsirler:
وَمَهَّدتُّ لَهُۥ تَمۡهِيدٗا
Ndipo ndamkonzera (ulemelero), kumkonzera (kwabwino).
Arapça tefsirler:
ثُمَّ يَطۡمَعُ أَنۡ أَزِيدَ
Kenako ali ndi dyera kuti ndimuonjezere (zina popanda kuthokoza).
Arapça tefsirler:
كَلَّآۖ إِنَّهُۥ كَانَ لِأٓيَٰتِنَا عَنِيدٗا
Koma sichoncho! Ndithu iye adali kutsutsa zizindikiro Zathu.
Arapça tefsirler:
سَأُرۡهِقُهُۥ صَعُودًا
Ndidzamkakamiza kuchilango chovuta; (kukwera phiri la ku Moto limene sakatha kulikwera).
Arapça tefsirler:
إِنَّهُۥ فَكَّرَ وَقَدَّرَ
Iye adalingalira (mu mtima mwake) ndi kukonza bwino (chonena chonyoza Qur’an).
Arapça tefsirler:
فَقُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Choncho waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Arapça tefsirler:
ثُمَّ قُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Ndiponso waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
Arapça tefsirler:
ثُمَّ نَظَرَ
Kenako adayang’anayang’ana (nkhope za anthu).
Arapça tefsirler:
ثُمَّ عَبَسَ وَبَسَرَ
Kenakonso adachita tsinya ndikukwinya nkhope (kwambiri ndi mkwiyo).
Arapça tefsirler:
ثُمَّ أَدۡبَرَ وَٱسۡتَكۡبَرَ
Kenakonso adanyoza choonadi ndi kudzikweza (posachivomereza),
Arapça tefsirler:
فَقَالَ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ يُؤۡثَرُ
Adati: “Sichina ichi (Qur’an) koma ndi matsenga amene adalandiridwa (kuchokera kwa amatsenga akale),
Arapça tefsirler:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا قَوۡلُ ٱلۡبَشَرِ
Sichina ichi koma ndi mawu a anthu!”
Arapça tefsirler:
سَأُصۡلِيهِ سَقَرَ
Posachedwa ndimlowetsa ku ‘Saqara.’
Arapça tefsirler:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سَقَرُ
Nanga ndi chiyani chingakudziwitse za ‘Saqara?’
Arapça tefsirler:
لَا تُبۡقِي وَلَا تَذَرُ
(Ndi moto umene) siusiya (mnofu) ndiponso siusiya (fupa),
Arapça tefsirler:
لَوَّاحَةٞ لِّلۡبَشَرِ
Wopsereza ndi kudetsa khungu.
Arapça tefsirler:
عَلَيۡهَا تِسۡعَةَ عَشَرَ
Kumeneko kuli khumi ndi asanu ndi anayi (alonda oyang’anira Motowo.)
Arapça tefsirler:
وَمَا جَعَلۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلنَّارِ إِلَّا مَلَٰٓئِكَةٗۖ وَمَا جَعَلۡنَا عِدَّتَهُمۡ إِلَّا فِتۡنَةٗ لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ لِيَسۡتَيۡقِنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَيَزۡدَادَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِيمَٰنٗا وَلَا يَرۡتَابَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَلِيَقُولَ ٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ وَٱلۡكَٰفِرُونَ مَاذَآ أَرَادَ ٱللَّهُ بِهَٰذَا مَثَلٗاۚ كَذَٰلِكَ يُضِلُّ ٱللَّهُ مَن يَشَآءُ وَيَهۡدِي مَن يَشَآءُۚ وَمَا يَعۡلَمُ جُنُودَ رَبِّكَ إِلَّا هُوَۚ وَمَا هِيَ إِلَّا ذِكۡرَىٰ لِلۡبَشَرِ
Ndipo sitidaike oyang’anira ku Moto (kukhala anthu) koma angelo; ndipo sitidaike chiwerengero chawo koma ndimayesero kwa amene sadakhulupirire, kuti atsimikize amene adapatsidwa mabuku (zimene Qur’an ikunena za chiwerengero cha angelo a ku Moto) ndiponso kuti chionjezeke chikhulupiliro kwa amene akhulupirira, ndikuti asapeneke amene adapatsidwa mabuku pamodzi ndi okhulupirira. Ndiponso kuti amene m’mitima mwawo muli matenda (matenda achinyengo) komanso osakhulupirira anene: “Kodi Allah akulinganji pa fanizo limeneli?” Momwemo Allah akumulekelera kusokera amene wamfuna, ndipo akumuongola amene wamfuna ndipo palibe amene angadziwe magulu a nkhondo a Mbuye wako kupatula Iye mwini. (Kutchula moto ndi zam’kati mwake) sichina koma ndichenjezo kwa anthu.
Arapça tefsirler:
كَلَّا وَٱلۡقَمَرِ
Sichoncho; ndikulumbilira mwezi,
Arapça tefsirler:
وَٱلَّيۡلِ إِذۡ أَدۡبَرَ
Ndi usiku pamene ukuchoka,
Arapça tefsirler:
وَٱلصُّبۡحِ إِذَآ أَسۡفَرَ
Ndi m’bandakucha pamene kukuyera.
Arapça tefsirler:
إِنَّهَا لَإِحۡدَى ٱلۡكُبَرِ
Ndithu uwo, (moto wa Jahannam) ndi chimodzi mwa malodza akulu,
Arapça tefsirler:
نَذِيرٗا لِّلۡبَشَرِ
Ndi chenjezo kwa anthu,
Arapça tefsirler:
لِمَن شَآءَ مِنكُمۡ أَن يَتَقَدَّمَ أَوۡ يَتَأَخَّرَ
Kwa yemwe wafuna mwa inu kutsogola (pochita zabwino zokamthandiza tsiku louka kwa akufa) kapena kutsalira (ndi za m’dziko).
Arapça tefsirler:
كُلُّ نَفۡسِۭ بِمَا كَسَبَتۡ رَهِينَةٌ
Mzimu uliwonse ukakhala chikole ndi zimene udachita.
Arapça tefsirler:
إِلَّآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡيَمِينِ
Kupatula akudzanja lamanja (Asilamu amene adadzimasula okha potembenukira kwa Allah).
Arapça tefsirler:
فِي جَنَّٰتٖ يَتَسَآءَلُونَ
(Iwo) adzakhala m’minda (yosasimbika kukongola kwake) akufunsana wina ndi mnzake,
Arapça tefsirler:
عَنِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Za anthu oipa,
Arapça tefsirler:
مَا سَلَكَكُمۡ فِي سَقَرَ
(Kuti): “Nchiyani chakulowetsani ku Moto?”
Arapça tefsirler:
قَالُواْ لَمۡ نَكُ مِنَ ٱلۡمُصَلِّينَ
Adzanena: “Sitidali m’gulu la omwe adali kupemphera (Swala).
Arapça tefsirler:
وَلَمۡ نَكُ نُطۡعِمُ ٱلۡمِسۡكِينَ
Ndiponso sitidali kuwadyetsa masikini.
Arapça tefsirler:
وَكُنَّا نَخُوضُ مَعَ ٱلۡخَآئِضِينَ
Koma tinkangomira (m’zachabe ndi zabodza) pamodzi ndi omira (m’menemo).
Arapça tefsirler:
وَكُنَّا نُكَذِّبُ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndiponso tidali kutsutsa za tsiku la malipiro.
Arapça tefsirler:
حَتَّىٰٓ أَتَىٰنَا ٱلۡيَقِينُ
Mpaka imfa idatifika.”
Arapça tefsirler:
فَمَا تَنفَعُهُمۡ شَفَٰعَةُ ٱلشَّٰفِعِينَ
Choncho siwudzawathandiza uwomboli wa awomboli.
Arapça tefsirler:
فَمَا لَهُمۡ عَنِ ٱلتَّذۡكِرَةِ مُعۡرِضِينَ
Kodi ali ndi chiyani iwo pakuti azinyozera chenjezoli (limene lili Qur’an?)
Arapça tefsirler:
كَأَنَّهُمۡ حُمُرٞ مُّسۡتَنفِرَةٞ
(Akuyenda mothamanga kuti asamve chenjezoli) ngati kuti iwo ndi mbidzi zothawa,
Arapça tefsirler:
فَرَّتۡ مِن قَسۡوَرَةِۭ
(Zimene) zikuthawa mkango.
Arapça tefsirler:
بَلۡ يُرِيدُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُؤۡتَىٰ صُحُفٗا مُّنَشَّرَةٗ
Ati akufuna aliyense mwa iwo apatsidwe kalata zotambasulidwa (zimene zitsimikize uthenga wa Mneneri Muhammad{s.a.w}).
Arapça tefsirler:
كَلَّاۖ بَل لَّا يَخَافُونَ ٱلۡأٓخِرَةَ
Sichoncho! Koma kuti iwo sakuopa tsiku lachimaliziro.
Arapça tefsirler:
كَلَّآ إِنَّهُۥ تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithu ichi (Qur’an) ndichikumbutso (chokwanira).
Arapça tefsirler:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Choncho amene wafuna achikumbukire (amene sakufuna ndizake)!
Arapça tefsirler:
وَمَا يَذۡكُرُونَ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُۚ هُوَ أَهۡلُ ٱلتَّقۡوَىٰ وَأَهۡلُ ٱلۡمَغۡفِرَةِ
Ndipo sangakumbukire pokhapokha Allah atafuna. Iye ndiye Amene ali woyenera kumuopa, ndiponso ndiye Mwini kukhululukira (amene akumuopa).
Arapça tefsirler:
 
Anlam tercümesi Sure: Sûretu'l-Muddessir
Surelerin fihristi Sayfa numarası
 
Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا - Mealler fihristi

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Kapat