அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அல்காஷியா   வசனம்:

ஸூரா அல்காஷியா

هَلۡ أَتَىٰكَ حَدِيثُ ٱلۡغَٰشِيَةِ
Kodi yakudzera, (iwe Mtumiki) (s.a.w) nkhani ya Qiyâma (imene idzaphimba anthu ndi zoopsa zake)?
அரபு விரிவுரைகள்:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٍ خَٰشِعَةٌ
Nkhope zina tsiku limenelo, zidzakhala zonyozeka,[425]
[425] Tanthauzo la nkhope apa ndi eni nkhopezo. Amene akunenedwa pamenepa ndi anthu oipa. Allah watchula nkhope chifukwa ndi chiwalo cholemekezeka pa chilengedwe cha munthu ndipo ndi pamene pali chithunzi chake.
அரபு விரிவுரைகள்:
عَامِلَةٞ نَّاصِبَةٞ
Zogwira ntchito yotopetsa kwambiri.
அரபு விரிவுரைகள்:
تَصۡلَىٰ نَارًا حَامِيَةٗ
Zikalowa ku Moto wotentha kwambiri.
அரபு விரிவுரைகள்:
تُسۡقَىٰ مِنۡ عَيۡنٍ ءَانِيَةٖ
Zikamwetsedwa mu kasupe wotentha kwabasi.
அரபு விரிவுரைகள்:
لَّيۡسَ لَهُمۡ طَعَامٌ إِلَّا مِن ضَرِيعٖ
Sadzakhala ndichakudya koma minga.
அரபு விரிவுரைகள்:
لَّا يُسۡمِنُ وَلَا يُغۡنِي مِن جُوعٖ
Yosanenepetsa (thupi) ndiponso yosathetsa njala.
அரபு விரிவுரைகள்:
وُجُوهٞ يَوۡمَئِذٖ نَّاعِمَةٞ
Nkhope zina tsiku limenelo zidzakhala zosangalala.
அரபு விரிவுரைகள்:
لِّسَعۡيِهَا رَاضِيَةٞ
Zidzakondwera ndi malipiro a zochita zake (za pa dziko lapansi).[426]
[426] Tanthauzo la “kukondweretsedwa ndi zochita zawo’’ ndikuti anthu abwino adzakondwera ndi ntchito zawo zabwino zomwe adazichita pa dziko lapansi akadzakhala ndi malipiro abwino pa tsiku lachimaliziro.
அரபு விரிவுரைகள்:
فِي جَنَّةٍ عَالِيَةٖ
M’minda ya pamwamba (Jannah).
அரபு விரிவுரைகள்:
لَّا تَسۡمَعُ فِيهَا لَٰغِيَةٗ
Sizikamva m’menemo mawu oipa, (otukwana ndi kulaula).
அரபு விரிவுரைகள்:
فِيهَا عَيۡنٞ جَارِيَةٞ
Mmenemo muli kasupe woyenda (mokongola).[427]
[427] (Ndime 12-16) Zosangalatsa zenizeni za tsiku lachimaliziro monga momwe adatiuzira Mneneri (s.a.w) kuti ku Jannah kuli zinthu zimene diso silidapenyepo ngakhale khutu silidamvepo ndipo sizidapitepo m’maganizo a munthu. Choncho zokondweretsa izi zimene Allah watiuza apa akungofanizira ndi zinthu zomwe tikuzidziwa.
அரபு விரிவுரைகள்:
فِيهَا سُرُرٞ مَّرۡفُوعَةٞ
Mmenemo muli makama a pamwamba,
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأَكۡوَابٞ مَّوۡضُوعَةٞ
Ndi zikho zoikidwa bwino (pamaso pawo),
அரபு விரிவுரைகள்:
وَنَمَارِقُ مَصۡفُوفَةٞ
Ndi misamiro yoikidwa bwino m’mizeremizere
அரபு விரிவுரைகள்:
وَزَرَابِيُّ مَبۡثُوثَةٌ
Ndi mphasa (zamtengo wapatali, carpet) zoyalidwa ponseponse.
அரபு விரிவுரைகள்:
أَفَلَا يَنظُرُونَ إِلَى ٱلۡإِبِلِ كَيۡفَ خُلِقَتۡ
Kodi (akunyozera kulingalira zisonyezo za Allah), sakulingalira kungamira idalengedwa motani?[428]
[428] (Ndime 17-20) Allah akuwauza kuti ayang’ane chilengedwe cha ngamira, thambo, mapiri ndi nthaka. Pambuyo pake alingalire, aone kuti amene adalenga zimenezo ngotha kuchita chilichonse monga kuukitsa anthu m’manda. Cholinga cha Allah potchula zinthu zimenezi, ngakhale kuti malangizowa nga munthu aliyense, koma adali kuwauza akafiri a pa Makka amene zinthu zimenezi maso awo ankaziona nthawi ndi nthawi.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِلَى ٱلسَّمَآءِ كَيۡفَ رُفِعَتۡ
Ndi thambo (limene akuliona nthawi zonse) m’mene lidatukulidwira (kutali popanda mzati)?
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِلَى ٱلۡجِبَالِ كَيۡفَ نُصِبَتۡ
Ndi mapiri momwe adakhazikitsidwira (molimba)?
அரபு விரிவுரைகள்:
وَإِلَى ٱلۡأَرۡضِ كَيۡفَ سُطِحَتۡ
Ndi nthaka momwe idayalidwira.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَذَكِّرۡ إِنَّمَآ أَنتَ مُذَكِّرٞ
Basi, kumbutsa (anthu) ndithu iwe, ndiwe mkumbutsi.
அரபு விரிவுரைகள்:
لَّسۡتَ عَلَيۡهِم بِمُصَيۡطِرٍ
Sindiwe wokakamiza anthu (kuti akhulupirire).[429]
[429] Ayah iyi ikukwana kuwatsutsa adani a Chisilamu amene akunena kuti, “chipembedzo cha Chisilamu chidafala ndi lupanga.” Kutanthauza kuti ankawakakamiza anthu kuti achivomere chipembedzochi. Sichodabwitsa kuona adani a Chisilamu akuchinyoza chipembedzochi, koma chodabwitsa nchakuti mawu onamawa nkumatulukanso mkamwa mwa anthu omwe amadzitcha kuti ndi Asilamu. Nzoona alipo ena mwa anthu odziwa za chipembedzo (ma Ulama) amene adanena kuti chipembedzo cha Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga. Koma simonga momwe akutanthauzilira adani amene sadziwa za Chisilamu nkumangotsatira mabodza a akuluakulu awo. Cholinga cha ma Ulama ponena kuti “Chisilamu chidatetezedwa ndi lupanga” kumeneko ndi kudziteteza kwa adani omwe adafuna kuchithetsa, osati kuwakakamiza anthu kulowa mchipembedzo. Kukakamiza anthu kulowa mChisilamu nkosaloledwa. Amene akudziwa mbiri ya Chisilamu, akudziwa kuti Asilamu sadalamulidwe kuchita Jihâd mpaka pamene akafiri adali kuwazunza. Pali nkhani zambiri za Maswahaba (otsatira Mneneri) (s.a.w) ku Madina pamene adafuna kuwakakamiza ana awo kulowa m’Chisilamu, koma Mneneri adawakaniza kutero. Basi, munthu amene akunena zoterezo mwina akutero pa chifukwa chosadziwa za chipembedzo cha Chisilamu, mwinanso nkukhala misala basi.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِلَّا مَن تَوَلَّىٰ وَكَفَرَ
Koma amene anyoza ndi kukanira (ulaliki wako),
அரபு விரிவுரைகள்:
فَيُعَذِّبُهُ ٱللَّهُ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَكۡبَرَ
Allah amulanga chilango chachikulu zedi.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّ إِلَيۡنَآ إِيَابَهُمۡ
Ndithu kobwerera kwawo ndi kwa Ife basi.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُمَّ إِنَّ عَلَيۡنَا حِسَابَهُم
Ndipo ndithu kuwerengedwa kwawo kuli kwa Ife.
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: ஸூரா அல்காஷியா
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

புனித அல் குர்ஆனுக்கான ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு- காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா மூலம் மொழிபெயர்க்கப்பட்டது.

மூடுக