قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ سورت: سورۂ معارج   آیت:

سورۂ معارج

سَأَلَ سَآئِلُۢ بِعَذَابٖ وَاقِعٖ
Wopempha adapempha kuti chiwadzere msanga chilango chopezekacho, (m’kupempha kwa chipongwe ndi kotsutsa).
عربی تفاسیر:
لِّلۡكَٰفِرِينَ لَيۡسَ لَهُۥ دَافِعٞ
Kwa okanira palibe angachitsekereze.
عربی تفاسیر:
مِّنَ ٱللَّهِ ذِي ٱلۡمَعَارِجِ
Chochokera kwa Allah Mwini makwelero.
عربی تفاسیر:
تَعۡرُجُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ وَٱلرُّوحُ إِلَيۡهِ فِي يَوۡمٖ كَانَ مِقۡدَارُهُۥ خَمۡسِينَ أَلۡفَ سَنَةٖ
Angelo ndi Jiburil amakwera kwa Iye (Allah) m’tsiku lomwe kutalika kwake kuli ngati zaka zikwi makumi asanu (50 000).
عربی تفاسیر:
فَٱصۡبِرۡ صَبۡرٗا جَمِيلًا
Choncho, pirira (iwe Mtumiki (s.a.w) kupirira kwabwino,
عربی تفاسیر:
إِنَّهُمۡ يَرَوۡنَهُۥ بَعِيدٗا
Ndithu iwo akuliona (tsiku la Qiyâma) kuti lili kutali (silingachitike).
عربی تفاسیر:
وَنَرَىٰهُ قَرِيبٗا
Koma Ife tikuliona kuti lilipafupi (ndilochitika).
عربی تفاسیر:
يَوۡمَ تَكُونُ ٱلسَّمَآءُ كَٱلۡمُهۡلِ
Tsiku limene thambo lidzakhala ngati mtovu wosungunuka.
عربی تفاسیر:
وَتَكُونُ ٱلۡجِبَالُ كَٱلۡعِهۡنِ
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya (wongouluka wokha).
عربی تفاسیر:
وَلَا يَسۡـَٔلُ حَمِيمٌ حَمِيمٗا
Ndipo m’bale sadzafunsa za m’bale wake.
عربی تفاسیر:
يُبَصَّرُونَهُمۡۚ يَوَدُّ ٱلۡمُجۡرِمُ لَوۡ يَفۡتَدِي مِنۡ عَذَابِ يَوۡمِئِذِۭ بِبَنِيهِ
Ngakhale adzawalole kuti aonane ndi kudziwana pakati pawo (sadzafunsana). Wochimwa adzalakalaka kuti akadaziwombola ku chilango cha tsiku limenelo ndi ana ake.
عربی تفاسیر:
وَصَٰحِبَتِهِۦ وَأَخِيهِ
Ndi mkazi wake, ndi m’bale wake.
عربی تفاسیر:
وَفَصِيلَتِهِ ٱلَّتِي تُـٔۡوِيهِ
Ndi akumtundu wake amene amamsunga.
عربی تفاسیر:
وَمَن فِي ٱلۡأَرۡضِ جَمِيعٗا ثُمَّ يُنجِيهِ
Ndi (kulipira) zonse za m’dziko, kuti zimpulumutse.
عربی تفاسیر:
كَلَّآۖ إِنَّهَا لَظَىٰ
Iyayi, (siya iwe wamachimo zimene ukulakalakazo)! Ndithu umenewu ndi Moto wa malawi.
عربی تفاسیر:
نَزَّاعَةٗ لِّلشَّوَىٰ
Wosupula mwamphamvu khungu.
عربی تفاسیر:
تَدۡعُواْ مَنۡ أَدۡبَرَ وَتَوَلَّىٰ
Udzaitana (potchula dzina la aliyense) amene adachitembenuzira msana choona ndi kunyoza.
عربی تفاسیر:
وَجَمَعَ فَأَوۡعَىٰٓ
Adasonkhanitsa (chuma) ndi kusunga (m’nkhokwe zake popanda kuperekera chopereka cha Allah).
عربی تفاسیر:
۞ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ خُلِقَ هَلُوعًا
Ndithu munthu walengedwa kukhala wosapirira.
عربی تفاسیر:
إِذَا مَسَّهُ ٱلشَّرُّ جَزُوعٗا
Mavuto akamkhudza amada nkhawa.
عربی تفاسیر:
وَإِذَا مَسَّهُ ٱلۡخَيۡرُ مَنُوعًا
Koma zabwino zikamkhudza amamana (ena ndi kuiwala mavuto amene adali nawo).
عربی تفاسیر:
إِلَّا ٱلۡمُصَلِّينَ
Kupatula opemphera Swala, (iwo alibe mbiri zoipazi).
عربی تفاسیر:
ٱلَّذِينَ هُمۡ عَلَىٰ صَلَاتِهِمۡ دَآئِمُونَ
Iwo amene sadukiza mapemphero awo a swala; (sakuwaleka ngakhale zivute chotani).
عربی تفاسیر:
وَٱلَّذِينَ فِيٓ أَمۡوَٰلِهِمۡ حَقّٞ مَّعۡلُومٞ
Ndi amene mchuma chawo muli gawo lodziwika (Zakaat),
عربی تفاسیر:
لِّلسَّآئِلِ وَٱلۡمَحۡرُومِ
La wopempha ndi wosapempha.
عربی تفاسیر:
وَٱلَّذِينَ يُصَدِّقُونَ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndi amene akuvomereza za tsiku la malipiro (ndi kumalikonzekera.)
عربی تفاسیر:
وَٱلَّذِينَ هُم مِّنۡ عَذَابِ رَبِّهِم مُّشۡفِقُونَ
Ndi iwo amene akuopa chilango chochokera kwa Mbuye wawo.
عربی تفاسیر:
إِنَّ عَذَابَ رَبِّهِمۡ غَيۡرُ مَأۡمُونٖ
Ndithu chilango cha Mbuye wawo nchosapulumuka nacho (munthu woipa).
عربی تفاسیر:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ لِفُرُوجِهِمۡ حَٰفِظُونَ
Ndiponso iwo amene akusunga umaliseche wawo (posachita chiwerewere),
عربی تفاسیر:
إِلَّا عَلَىٰٓ أَزۡوَٰجِهِمۡ أَوۡ مَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُهُمۡ فَإِنَّهُمۡ غَيۡرُ مَلُومِينَ
Kupatula kwa akazi awo ndi amene manja awo akumanja apeza; ndithu pazimenezo iwo sangadzudzulidwe.
عربی تفاسیر:
فَمَنِ ٱبۡتَغَىٰ وَرَآءَ ذَٰلِكَ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡعَادُونَ
Koma amene angafune (zina) kusiya zimenezi iwowo ndiwo olumpha malire.
عربی تفاسیر:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ لِأَمَٰنَٰتِهِمۡ وَعَهۡدِهِمۡ رَٰعُونَ
Ndi iwo amene amasunga mwaubwino zimene amasungitsidwa ndi zimene alonjeza.
عربی تفاسیر:
وَٱلَّذِينَ هُم بِشَهَٰدَٰتِهِمۡ قَآئِمُونَ
Ndi iwo amene amaima molungama popereka umboni wawo.
عربی تفاسیر:
وَٱلَّذِينَ هُمۡ عَلَىٰ صَلَاتِهِمۡ يُحَافِظُونَ
Ndiponso iwo amene amasunga (mwaubwino) mapemphero awo a swala.
عربی تفاسیر:
أُوْلَٰٓئِكَ فِي جَنَّٰتٖ مُّكۡرَمُونَ
Amene ali ndi mbiri zimenezi adzakhala m’Minda (yamtendere) ali olemekezedwa.
عربی تفاسیر:
فَمَالِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ قِبَلَكَ مُهۡطِعِينَ
Kodi kuli chiyani kwa amene akana (chikhulupiliro) akuthamangira kwa iwe (maso ali pamtunda)?
عربی تفاسیر:
عَنِ ٱلۡيَمِينِ وَعَنِ ٱلشِّمَالِ عِزِينَ
Atakuzungulira ena chakumanja ena chakumanzere.
عربی تفاسیر:
أَيَطۡمَعُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُدۡخَلَ جَنَّةَ نَعِيمٖ
Kodi akulakalaka aliyense mwa iwo kuti akalowetsedwe ku Munda wamtendere?
عربی تفاسیر:
كَلَّآۖ إِنَّا خَلَقۡنَٰهُم مِّمَّا يَعۡلَمُونَ
Asiye (kukhumba kwawo kokalowa ku Munda wamtendere)! Ndithu Ife tidawalenga kuchokera m’zimene akudziwa (madzi opanda pake).
عربی تفاسیر:
فَلَآ أُقۡسِمُ بِرَبِّ ٱلۡمَشَٰرِقِ وَٱلۡمَغَٰرِبِ إِنَّا لَقَٰدِرُونَ
Ndikulumbilira Mbuye wa kuvuma ndi kuzambwe konse ndithu Ndife Wokhoza.
عربی تفاسیر:
عَلَىٰٓ أَن نُّبَدِّلَ خَيۡرٗا مِّنۡهُمۡ وَمَا نَحۡنُ بِمَسۡبُوقِينَ
Kuwasintha ndi kudzetsa abwino kuposa iwo; Ife palibe (chilichonse) chotipambana.
عربی تفاسیر:
فَذَرۡهُمۡ يَخُوضُواْ وَيَلۡعَبُواْ حَتَّىٰ يُلَٰقُواْ يَوۡمَهُمُ ٱلَّذِي يُوعَدُونَ
Asiye azingolankhula zopanda pake ndi kumangosewera mpaka adzakumane ndi tsiku lawo limene akulonjezedwa.
عربی تفاسیر:
يَوۡمَ يَخۡرُجُونَ مِنَ ٱلۡأَجۡدَاثِ سِرَاعٗا كَأَنَّهُمۡ إِلَىٰ نُصُبٖ يُوفِضُونَ
Tsiku limene adzatuluke m’manda uku akuthamanga (kudza kwa woitana) ngati kuti akuthamangira kumafano awo (amene adali kuwapembedza).
عربی تفاسیر:
خَٰشِعَةً أَبۡصَٰرُهُمۡ تَرۡهَقُهُمۡ ذِلَّةٞۚ ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلَّذِي كَانُواْ يُوعَدُونَ
Maso awo ali zyoli, (osatha kuwakweza); kuyaluka kutawaphimba! Limenelo ndilo tsiku lomwe adali kulonjezedwa (pomwe adali padziko lapansi.
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ سورت: سورۂ معارج
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - شیشیوا ترجمہ۔ - ترجمے کی لسٹ

قرآن کریم کے معانی کا شیشیوا ترجمہ، ترجمہ خالد ابراہیم بيتلا نے کیا ہے۔نسخہ ۲۰۲۰م۔

بند کریں