কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ * - অনুবাদসমূহের সূচী


অর্থসমূহের অনুবাদ সূরা: সূরা আন-নাবা   আয়াত:

সূরা আন-নাবা

عَمَّ يَتَسَآءَلُونَ
۞ Kodi akufunsana zachiyani?
আরবি তাফসীরসমূহ:
عَنِ ٱلنَّبَإِ ٱلۡعَظِيمِ
Za nkhani yayikulu ija.
আরবি তাফসীরসমূহ:
ٱلَّذِي هُمۡ فِيهِ مُخۡتَلِفُونَ
Imene iwo akusiyana (maganizo).[372]
[372] Nkhani yaikulu imene akafiri (anthu osakhulupilira Allah) adali kufunsana wina ndi mnzake ndi nkhani yakuuka tsiku la Qiyâma ndi uneneri wa Mtumiki Muhammad. Amafunsana kuti, “Kodi nzoona tidzauka m’manda, nanga nzoona kuti Muhammad ndi Mneneri?” Adali kufunsananso kuti, “Kodi zakuti Allah ndi Mmodzi ndi zoona?”
আরবি তাফসীরসমূহ:
كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Aleke (zimenezo) adzadziwa posachedwapa.[373]
[373] Kuyankhula koti: “Kallaa” kwanenedwa kwambiri m’Qur’an. Tanthauzo lake nthawi zina ndikuletsa, nthawi zina ndikutsimikiza. Choncho mawuwa amatanthauzidwa malinga ndi momwe chiganizocho chilili.
আরবি তাফসীরসমূহ:
ثُمَّ كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Ayi, ndithu aleke (zimenezo); posachedwapa adzadziwa zoona zake (pamene chilango chidzawatsikira).[374]
[374] Allah, apa, akuwauza kuti asiye kuganizira zinthu zopanda pake. Kodi sadadziwebe mpaka pano kuti Muhammad ndi Mneneri wa Allah, ndikuti Allah ndi Mmodzi yekha? Ndikutinso kuli tsiku lachimaliziro; pamene munthu aliyense adzalipidwa pa zimene adachita? Basi tsiku lachimaliziro likadzawafikira adzadziwa kuti zimene adali kuwauza Mneneri nzoona.
আরবি তাফসীরসমূহ:
أَلَمۡ نَجۡعَلِ ٱلۡأَرۡضَ مِهَٰدٗا
Kodi sitidachite nthaka kukhala ngati choyala?[375]
[375] Kuyambira Ayah iyi, kudzafika Ayah 16, Allah akusonyeza anthu Ake madalitso ambiri omwe wawadalitsa nawo kuti azindikire kuti Mwini kupereka madalitso amenewa m’dziko sangawasiye anthu Ake m’kusokera popanda kuwatumizira munthu wowaongolera ku njira yabwino, ndikuwadziwitsa zamtendere wapadziko ndi tsiku lachimaliziro. Ndikuti Allah amene adapanga zonsezi palibe chimene angachilephere. Ndipo tanthauzo la choyala, apa, ndi pamalo poti nkutheka munthu kuchita chimene akufuna pa moyo wake. Tanthauzo lake sikuti dothi lakhala ngati mkeka wa pabedi ayi.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَٱلۡجِبَالَ أَوۡتَادٗا
Ndi mapiri ngati zichiri (zolimbitsa nthaka)?
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَخَلَقۡنَٰكُمۡ أَزۡوَٰجٗا
Ndipo takulengani mitundu iwiri (amuna ndi akazi).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَجَعَلۡنَا نَوۡمَكُمۡ سُبَاتٗا
Ndipo tidachita tulo tanu kukhala mpumulo (ku mavuto a ntchito).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَجَعَلۡنَا ٱلَّيۡلَ لِبَاسٗا
Ndipo taupanga usiku kukhala ngati chovala (pokuvindikirani ndi mdima wake).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَجَعَلۡنَا ٱلنَّهَارَ مَعَاشٗا
Ndipo tapanga masana kukhala nthawi yopezera zofunika pa moyo;
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَبَنَيۡنَا فَوۡقَكُمۡ سَبۡعٗا شِدَادٗا
Ndipo tamanga pamwamba panu thambo zisanu ndi ziwiri zolimba;
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَجَعَلۡنَا سِرَاجٗا وَهَّاجٗا
Ndipo tidapanga nyali yowala ndi yotentha kwambiri (dzuwa);
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَأَنزَلۡنَا مِنَ ٱلۡمُعۡصِرَٰتِ مَآءٗ ثَجَّاجٗا
Ndipo tawatsitsa madzi otsika mwamphamvu kuchokera ku mitambo, ya mvula;
আরবি তাফসীরসমূহ:
لِّنُخۡرِجَ بِهِۦ حَبّٗا وَنَبَاتٗا
Kuti titulutse ndi madziwo mbewu ndi m’mera, (chomwe ndi chakudya cha anthu ndi nyama).
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَجَنَّٰتٍ أَلۡفَافًا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo.
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنَّ يَوۡمَ ٱلۡفَصۡلِ كَانَ مِيقَٰتٗا
Ndithu tsiku la chiweruziro ndinthawi imene idakhazikitsidwa kale.
আরবি তাফসীরসমূহ:
يَوۡمَ يُنفَخُ فِي ٱلصُّورِ فَتَأۡتُونَ أَفۡوَاجٗا
Tsiku limene lipenga (lakuuka) lidzaimbidwa ndipo inu mudzabwera (kubwalo losonkhanirana) muli magulumagulu.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَفُتِحَتِ ٱلسَّمَآءُ فَكَانَتۡ أَبۡوَٰبٗا
Ndipo thambo lidzatsegulidwa (mbali zonse): choncho lidzakhala makomomakomo.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَسُيِّرَتِ ٱلۡجِبَالُ فَكَانَتۡ سَرَابًا
Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake, adzakhala ngati zideruderu.[376]
[376] Apa, ndikuti zimene munthu amaziona patsogolo pake nkumaziganizira ngati madzi pomwe sali madzi. Choncho pa tsiku limenelo mapiri adzaoneka ngati akhazikika monga m’mene adalili pomwe sichoncho, adzakhala ngati thonje louluka ndi mphepo.
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتۡ مِرۡصَادٗا
Ndithu moto wa Jahannam ukuwadikilira (oipa).
আরবি তাফসীরসমূহ:
لِّلطَّٰغِينَ مَـَٔابٗا
Mbuto ya opyola malire.[377]
[377] Jahannam ndi dzina lamoto wodziwika wa tsiku lachimaliziro. Apa Allah akutidziwitsa kuti Jahannam ndi malo amene akudikira akafiri kuti m’menemo akalipidwe malipiro awo chifukwa chokanira aneneri pambuyo powasonyeza zizindikiro zoti iwo ndi aneneri a Allah. Ndiponso kumulakwira Allah pochita zimene adaletsa monga; kukana umodzi wa Allah, kukana utumiki wa Mahammad (s.a.w) ndi kukana uthenga wa Qur’an. Komanso kugwa mmachimo osiyanasiyana.
আরবি তাফসীরসমূহ:
لَّٰبِثِينَ فِيهَآ أَحۡقَابٗا
Adzakhala m’menemo muyaya.
আরবি তাফসীরসমূহ:
لَّا يَذُوقُونَ فِيهَا بَرۡدٗا وَلَا شَرَابًا
Sadzalawa m’menemo kuzizira (kowachotsera kutentha), kapena chakumwa (chowachotsera ludzu lawo);
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِلَّا حَمِيمٗا وَغَسَّاقٗا
Kupatula madzi otentha kwambiri ndi mafinya (otuluka mmatupi a anthu a ku Moto);
আরবি তাফসীরসমূহ:
جَزَآءٗ وِفَاقًا
Kukhala malipiro olingana ndi ntchito zawo.
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنَّهُمۡ كَانُواْ لَا يَرۡجُونَ حِسَابٗا
Ndithu iwo sadali kuyembekezera chiwerengero (cha Allah);
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَكَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا كِذَّابٗا
Adatsutsa zizindikiro Zathu (zosonyeza kuuka kwa akufa) ndi mtsutso waukulu.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَكُلَّ شَيۡءٍ أَحۡصَيۡنَٰهُ كِتَٰبٗا
Ndipo chinthu chilichonse tachisunga mochilemba.
আরবি তাফসীরসমূহ:
فَذُوقُواْ فَلَن نَّزِيدَكُمۡ إِلَّا عَذَابًا
Basi, lawani (lero chilango Changa); sitikuonjezerani chinthu china koma chilango pamwamba pa chilango.
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ مَفَازًا
Ndithu anthu oopa Allah adzakhala ndi malo wopambana.
আরবি তাফসীরসমূহ:
حَدَآئِقَ وَأَعۡنَٰبٗا
Minda ndi zipatso za mphesa.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَكَوَاعِبَ أَتۡرَابٗا
Ndi mabuthu (anamwali) ofanana misinkhu.
আরবি তাফসীরসমূহ:
وَكَأۡسٗا دِهَاقٗا
Ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa.
আরবি তাফসীরসমূহ:
لَّا يَسۡمَعُونَ فِيهَا لَغۡوٗا وَلَا كِذَّٰبٗا
Sakamva m’menemo mawu opanda pake kapena bodza.
আরবি তাফসীরসমূহ:
جَزَآءٗ مِّن رَّبِّكَ عَطَآءً حِسَابٗا
Amenewa ndi malipiro ochokera kwa Mbuye wako zopereka zokwanira.[378]
[378] Chipembedzo cha Chisilamu chikuphunzitsa kuti pali zisangalalo ziwiri: Chisangalalo cha mzimu ndi chisangalalo cha thupi. Tsono chisangalalo cha mzimu ndiko kuyanjana kochokera kwa Allah kumene anthu Ake abwino adzakupeza. Chisangalalo cha thupi ndi monga m’mene afotokozera mu Ayah iyi ndi msura zina. Zokondweretsa monga minda, akazi okongola, mowa (osaledzeretsa) ndiponso sikudzakhala kumva chilichonse chokhumudwitsa.
Taonani, zoledzeretsa ndi zoletsedwa padziko lino lapansi chifukwa cha zoipa zake. Koma mowa wa patsiku la Qiyâma udzakhala wopanda zoipa.
আরবি তাফসীরসমূহ:
رَّبِّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا ٱلرَّحۡمَٰنِۖ لَا يَمۡلِكُونَ مِنۡهُ خِطَابٗا
Mbuye wa kumwamba ndi pansi ndi zimene zili pakati pake; Wachifundo chambiri. Palibe amene adzakhala ndi mphamvu yolankhulana naye (pa tsiku limenero);
আরবি তাফসীরসমূহ:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلرُّوحُ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ صَفّٗاۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنۡ أَذِنَ لَهُ ٱلرَّحۡمَٰنُ وَقَالَ صَوَابٗا
Tsiku limene adzaima Jibril ndi angelo pa mzere (ali odzichepetsa); sadzayankhula aliyense mwa iwo kupatula yekhayo amene adzaloledwa ndi (Allah) Wachifundo chambiri (kuyankhula) ndipo adzanena zolondola.
আরবি তাফসীরসমূহ:
ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلۡحَقُّۖ فَمَن شَآءَ ٱتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِۦ مَـَٔابًا
Limenelo ndi tsiku loona, (lopanda chikaiko); choncho amene akufuna adzipezere malo (njira yonkera) kwa Mbuye wake. (Pomugonjera Iye pa moyo uno wadziko lapansi).
আরবি তাফসীরসমূহ:
إِنَّآ أَنذَرۡنَٰكُمۡ عَذَابٗا قَرِيبٗا يَوۡمَ يَنظُرُ ٱلۡمَرۡءُ مَا قَدَّمَتۡ يَدَاهُ وَيَقُولُ ٱلۡكَافِرُ يَٰلَيۡتَنِي كُنتُ تُرَٰبَۢا
Ndithu tikukuchenjezani zachilango chomwe chili pafupi kudza; tsiku limene munthu adzayang’ana zimene adatsogoza manja ake, ndipo wosakhulupirira adzanena: Kalanga ine! Ndikadakhala dothi, (kuti ndisalangidwe chilango chikundiyembekezachi).
আরবি তাফসীরসমূহ:
 
অর্থসমূহের অনুবাদ সূরা: সূরা আন-নাবা
সূরাসমূহের সূচী পৃষ্ঠার নাম্বার
 
কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ - চেওয়া ভাষায় অনুবাদ - অনুবাদসমূহের সূচী

চেওয়া ভাষা আল-কুরআনুল কারীমের অর্থসমূহের অনুবাদ-খালিদ ইবরাহীম বীতালা, সংস্করণ ২০২০ খ্রি.

বন্ধ