Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo * - Tippudi firooji ɗii


Firo maanaaji Simoore: Simoore ɓaaƴo (al-humasa)   Aaya:

Simoore ɓaaƴo (al-humasa)

وَيۡلٞ لِّكُلِّ هُمَزَةٖ لُّمَزَةٍ
Kuonongeka koopsa kudzampeza aliyense wojeda ndi wonyoza anthu polozera (ndi maso kapena kuyankhula ndi lirime).[482]
[482] Kujeda kwa mtundu uliwonse ndi koipa. Anthu ambiri amaganiza kuti kujeda ndi chinthu chochepa, saona kuti ndi chinthu choipa, pomwe Qur’an ikuletsa kwatunthu mpaka mwakuti imamufanizira munthu wojeda ngati munthu yemwe amadya minofu ya mnzake wakufa. Mu Ayah imeneyi, Allah wanena kuti “Wayilun” lomwe tanthauzo lake ndi “Kuonongeka koopsa.” Choncho nkofunika kwa munthu aliyense kupewa khalidwe lojeda.
Faccirooji aarabeeji:
ٱلَّذِي جَمَعَ مَالٗا وَعَدَّدَهُۥ
Yemwe wasonkhanitsa chuma ndikumachiwerengera.[483]
[483] Mmenemo ndi momwe alili munthu wa umbombo, kukoma kwa chuma kwa iye, ndikuchisonkhanitsa ndikumachiwerengera akakhala ndi danga; sikuti akufuna kudziwa kuchuluka kwake koma kungokondweretsedwa ndikuchiwerengako. Saganizira zimene zingamuthandize iye mwini kapena kuthandiza anzake.
Chuma ntchito yake ndikuti chimthandize mwini chumacho pa zinthu zabwino zosiyanasiyana pamodzi ndi anzake, osati kungochikhazika ndikumangochiwerengera mokhumbiza ena.
Faccirooji aarabeeji:
يَحۡسَبُ أَنَّ مَالَهُۥٓ أَخۡلَدَهُۥ
Akuganiza kuti chuma chakecho chimkhazika (pa dziko) nthawi yaitali (ndikumteteza ku zimene sakuzifuna).
Faccirooji aarabeeji:
كَلَّاۖ لَيُنۢبَذَنَّ فِي ٱلۡحُطَمَةِ
Sichoncho! (Asiye maganizo amenewo) ndithudi, akaponyedwa ku Moto woononga (chifukwa cha kuipa kwa zochita zake).
Faccirooji aarabeeji:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡحُطَمَةُ
Ndi chiyani chingakudziwitse za Moto woonongawu?
Faccirooji aarabeeji:
نَارُ ٱللَّهِ ٱلۡمُوقَدَةُ
Umenewu ndi Moto wa Allah woyaka (nthawi zonse, woononga chilichonse choponyedwa mmenemo).
Faccirooji aarabeeji:
ٱلَّتِي تَطَّلِعُ عَلَى ٱلۡأَفۡـِٔدَةِ
Umene umakwera mpaka ku mtima.[484]
[484] Moto umenewu, sukapsereza kunja kokha, ukapsereza mpaka ndi mu mtima momwe.
Faccirooji aarabeeji:
إِنَّهَا عَلَيۡهِم مُّؤۡصَدَةٞ
Ndithu motowo ukawazinga (ndi kuwatsekera makomo).
Faccirooji aarabeeji:
فِي عَمَدٖ مُّمَدَّدَةِۭ
Munsanamira za zitalizitali (kotero kuti sakatha kugwedezeka mmenemo kapena kupulumuka).
Faccirooji aarabeeji:
 
Firo maanaaji Simoore: Simoore ɓaaƴo (al-humasa)
Tippudi cimooje Tonngoode hello ngoo
 
Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo - Tippudi firooji ɗii

Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo fayde e ɗemngal siisii, fari ɗum ko Kaaliid piitalaa. Tummbutere hitaande 2020

Uddude