Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Sūra: Sūra Ad-Duchaa   Aja (Korano eilutė):

Sūra Ad-Duchaa

وَٱلضُّحَىٰ
Ndikulumbilira mmawa dzuwa litakwera (imene ili nthawi yantchito),
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا سَجَىٰ
Ndi usiku pamene ukuvindikira.
Tafsyrai arabų kalba:
مَا وَدَّعَكَ رَبُّكَ وَمَا قَلَىٰ
Sadakusiye Mbuye wako (iwe Mneneri) (s.a.w) ndiponso sadakude.[452]
[452] M’masiku oyamba pa chiyambi cha Usilamu, padapita masiku angapo Mtumiki (s.a.w) osamutsikira chivumbulutso. Iye poona izi adali kukaika ndi kudandaula kwakukulu, nao okanira a pa Makka adali kumchita chipongwe. Adali kumunena kuti: “Kodi Mbuye wako wakusiya kapena wakukwiira?’’ Basi apa Allah akumutonthoza Mneneri Wake, pamodzi ndi kuwayankha okanira aja kuti: “Sadamusiye ndipo sadakwiye naye.”
Tafsyrai arabų kalba:
وَلَلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ لَّكَ مِنَ ٱلۡأُولَىٰ
Ndithu moyo watsiku lirimkudza ndi wabwino kwa iwe kuposa umoyo woyambawu.
Tafsyrai arabų kalba:
وَلَسَوۡفَ يُعۡطِيكَ رَبُّكَ فَتَرۡضَىٰٓ
Ndithu posachedwapa akupatsa Mbuye wako (zabwino zamdziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro) ndipo ukondwera.[453]
[453] Zopatsidwa zomwe adalonjezedwa apa ndi Allah, ndi zapadziko mpaka kumwamba (Akhera). Padziko lapansi adampatsa chilichonse chimene adali kuchilakalaka monga kuwaongola anthu ake, kuchilemekeza chipembedzo chake ndi kuwagonjetsa adani ake. Zonsezi Allah adamchitira mnyengo yochepa modabwitsa.
Tafsyrai arabų kalba:
أَلَمۡ يَجِدۡكَ يَتِيمٗا فَـَٔاوَىٰ
Kodi sadakupeze uli wa masiye ndipo adakupatsa pokhala pabwino?
Tafsyrai arabų kalba:
وَوَجَدَكَ ضَآلّٗا فَهَدَىٰ
Ndipo adakupeza uli wosazindikira (Qur’an) nakuongola (pokuzindikiritsa Qur’aniyo ndi malamulo a chipembedzo)?[454]
[454] Mneneri Muhammad (s.a.w) asanapatsidwe uneneri wake ndi Allah anali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira yachiongoko.
Tafsyrai arabų kalba:
وَوَجَدَكَ عَآئِلٗا فَأَغۡنَىٰ
Ndiponso adakupeza uli wosauka nakulemeretsa?
Tafsyrai arabų kalba:
فَأَمَّا ٱلۡيَتِيمَ فَلَا تَقۡهَرۡ
Basi, wamasiye usamchitire nkhanza.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَمَّا ٱلسَّآئِلَ فَلَا تَنۡهَرۡ
Ndiponso wopempha usamukalipire.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَمَّا بِنِعۡمَةِ رَبِّكَ فَحَدِّثۡ
Tsono mtendere wa Mbuye wako uwutchule (pothokoza ndi kugwira ntchito zabwino).
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Sūra: Sūra Ad-Duchaa
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas - Vertimų turinys

Kilniojo Korano reikšmių vertimas į čevų k., išvertė Khaled Ibrahim Betala. 2020 m. leidimas.

Uždaryti