แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา * - สารบัญ​คำแปล


แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: Al-Muddaththir   อายะฮ์:

Al-Muddaththir

يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمُدَّثِّرُ
E iwe wadziphimba (nsalu)!
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
قُمۡ فَأَنذِرۡ
Imilira ndipo uwachenjeze (anthu za chilango cha Allah).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَرَبَّكَ فَكَبِّرۡ
Ndipo Mbuye wako (Yekha) umkulitse (pomulemekeza).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَثِيَابَكَ فَطَهِّرۡ
Ndipo nsalu zako uziyeretse (ndi madzi ku uve).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَٱلرُّجۡزَ فَٱهۡجُرۡ
Ndiponso zoipa (monga mafano ndi zina zonse ) zipewe.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَلَا تَمۡنُن تَسۡتَكۡثِرُ
Usapatse (anthu) ncholinga choti ulandire zambiri.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَلِرَبِّكَ فَٱصۡبِرۡ
Chifukwa cha Mbuye wako, pirira (ku malamulo Ake poleka zomwe waletsa ndi kuchita zimene walamula).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَإِذَا نُقِرَ فِي ٱلنَّاقُورِ
Ndipo likadzaimbidwa lipenga,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَذَٰلِكَ يَوۡمَئِذٖ يَوۡمٌ عَسِيرٌ
Tsiku limenelo lidzakhala tsiku lovuta.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
عَلَى ٱلۡكَٰفِرِينَ غَيۡرُ يَسِيرٖ
Kwa osakhulupirira, silidzakhala lofewa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ذَرۡنِي وَمَنۡ خَلَقۡتُ وَحِيدٗا
Ndisiye ndiamene ndidamlenga Ndekha,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَجَعَلۡتُ لَهُۥ مَالٗا مَّمۡدُودٗا
Ndipo ndampatsa chuma chambiri.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَبَنِينَ شُهُودٗا
Ndi ana okhala nawo (paliponse).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَهَّدتُّ لَهُۥ تَمۡهِيدٗا
Ndipo ndamkonzera (ulemelero), kumkonzera (kwabwino).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ يَطۡمَعُ أَنۡ أَزِيدَ
Kenako ali ndi dyera kuti ndimuonjezere (zina popanda kuthokoza).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّآۖ إِنَّهُۥ كَانَ لِأٓيَٰتِنَا عَنِيدٗا
Koma sichoncho! Ndithu iye adali kutsutsa zizindikiro Zathu.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
سَأُرۡهِقُهُۥ صَعُودًا
Ndidzamkakamiza kuchilango chovuta; (kukwera phiri la ku Moto limene sakatha kulikwera).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنَّهُۥ فَكَّرَ وَقَدَّرَ
Iye adalingalira (mu mtima mwake) ndi kukonza bwino (chonena chonyoza Qur’an).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَقُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Choncho waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ قُتِلَ كَيۡفَ قَدَّرَ
Ndiponso waonongeka! Adakonza bwanji (poinyoza Qur’an)!
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ نَظَرَ
Kenako adayang’anayang’ana (nkhope za anthu).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ عَبَسَ وَبَسَرَ
Kenakonso adachita tsinya ndikukwinya nkhope (kwambiri ndi mkwiyo).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ أَدۡبَرَ وَٱسۡتَكۡبَرَ
Kenakonso adanyoza choonadi ndi kudzikweza (posachivomereza),
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَقَالَ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ يُؤۡثَرُ
Adati: “Sichina ichi (Qur’an) koma ndi matsenga amene adalandiridwa (kuchokera kwa amatsenga akale),
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا قَوۡلُ ٱلۡبَشَرِ
Sichina ichi koma ndi mawu a anthu!”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
سَأُصۡلِيهِ سَقَرَ
Posachedwa ndimlowetsa ku ‘Saqara.’
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سَقَرُ
Nanga ndi chiyani chingakudziwitse za ‘Saqara?’
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
لَا تُبۡقِي وَلَا تَذَرُ
(Ndi moto umene) siusiya (mnofu) ndiponso siusiya (fupa),
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
لَوَّاحَةٞ لِّلۡبَشَرِ
Wopsereza ndi kudetsa khungu.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
عَلَيۡهَا تِسۡعَةَ عَشَرَ
Kumeneko kuli khumi ndi asanu ndi anayi (alonda oyang’anira Motowo.)
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَا جَعَلۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلنَّارِ إِلَّا مَلَٰٓئِكَةٗۖ وَمَا جَعَلۡنَا عِدَّتَهُمۡ إِلَّا فِتۡنَةٗ لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ لِيَسۡتَيۡقِنَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَيَزۡدَادَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِيمَٰنٗا وَلَا يَرۡتَابَ ٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَلِيَقُولَ ٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ وَٱلۡكَٰفِرُونَ مَاذَآ أَرَادَ ٱللَّهُ بِهَٰذَا مَثَلٗاۚ كَذَٰلِكَ يُضِلُّ ٱللَّهُ مَن يَشَآءُ وَيَهۡدِي مَن يَشَآءُۚ وَمَا يَعۡلَمُ جُنُودَ رَبِّكَ إِلَّا هُوَۚ وَمَا هِيَ إِلَّا ذِكۡرَىٰ لِلۡبَشَرِ
Ndipo sitidaike oyang’anira ku Moto (kukhala anthu) koma angelo; ndipo sitidaike chiwerengero chawo koma ndimayesero kwa amene sadakhulupirire, kuti atsimikize amene adapatsidwa mabuku (zimene Qur’an ikunena za chiwerengero cha angelo a ku Moto) ndiponso kuti chionjezeke chikhulupiliro kwa amene akhulupirira, ndikuti asapeneke amene adapatsidwa mabuku pamodzi ndi okhulupirira. Ndiponso kuti amene m’mitima mwawo muli matenda (matenda achinyengo) komanso osakhulupirira anene: “Kodi Allah akulinganji pa fanizo limeneli?” Momwemo Allah akumulekelera kusokera amene wamfuna, ndipo akumuongola amene wamfuna ndipo palibe amene angadziwe magulu a nkhondo a Mbuye wako kupatula Iye mwini. (Kutchula moto ndi zam’kati mwake) sichina koma ndichenjezo kwa anthu.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّا وَٱلۡقَمَرِ
Sichoncho; ndikulumbilira mwezi,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَٱلَّيۡلِ إِذۡ أَدۡبَرَ
Ndi usiku pamene ukuchoka,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَٱلصُّبۡحِ إِذَآ أَسۡفَرَ
Ndi m’bandakucha pamene kukuyera.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنَّهَا لَإِحۡدَى ٱلۡكُبَرِ
Ndithu uwo, (moto wa Jahannam) ndi chimodzi mwa malodza akulu,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
نَذِيرٗا لِّلۡبَشَرِ
Ndi chenjezo kwa anthu,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
لِمَن شَآءَ مِنكُمۡ أَن يَتَقَدَّمَ أَوۡ يَتَأَخَّرَ
Kwa yemwe wafuna mwa inu kutsogola (pochita zabwino zokamthandiza tsiku louka kwa akufa) kapena kutsalira (ndi za m’dziko).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كُلُّ نَفۡسِۭ بِمَا كَسَبَتۡ رَهِينَةٌ
Mzimu uliwonse ukakhala chikole ndi zimene udachita.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِلَّآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡيَمِينِ
Kupatula akudzanja lamanja (Asilamu amene adadzimasula okha potembenukira kwa Allah).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فِي جَنَّٰتٖ يَتَسَآءَلُونَ
(Iwo) adzakhala m’minda (yosasimbika kukongola kwake) akufunsana wina ndi mnzake,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
عَنِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Za anthu oipa,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مَا سَلَكَكُمۡ فِي سَقَرَ
(Kuti): “Nchiyani chakulowetsani ku Moto?”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
قَالُواْ لَمۡ نَكُ مِنَ ٱلۡمُصَلِّينَ
Adzanena: “Sitidali m’gulu la omwe adali kupemphera (Swala).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَلَمۡ نَكُ نُطۡعِمُ ٱلۡمِسۡكِينَ
Ndiponso sitidali kuwadyetsa masikini.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَكُنَّا نَخُوضُ مَعَ ٱلۡخَآئِضِينَ
Koma tinkangomira (m’zachabe ndi zabodza) pamodzi ndi omira (m’menemo).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَكُنَّا نُكَذِّبُ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Ndiponso tidali kutsutsa za tsiku la malipiro.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
حَتَّىٰٓ أَتَىٰنَا ٱلۡيَقِينُ
Mpaka imfa idatifika.”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَمَا تَنفَعُهُمۡ شَفَٰعَةُ ٱلشَّٰفِعِينَ
Choncho siwudzawathandiza uwomboli wa awomboli.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَمَا لَهُمۡ عَنِ ٱلتَّذۡكِرَةِ مُعۡرِضِينَ
Kodi ali ndi chiyani iwo pakuti azinyozera chenjezoli (limene lili Qur’an?)
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَأَنَّهُمۡ حُمُرٞ مُّسۡتَنفِرَةٞ
(Akuyenda mothamanga kuti asamve chenjezoli) ngati kuti iwo ndi mbidzi zothawa,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَرَّتۡ مِن قَسۡوَرَةِۭ
(Zimene) zikuthawa mkango.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
بَلۡ يُرِيدُ كُلُّ ٱمۡرِيٕٖ مِّنۡهُمۡ أَن يُؤۡتَىٰ صُحُفٗا مُّنَشَّرَةٗ
Ati akufuna aliyense mwa iwo apatsidwe kalata zotambasulidwa (zimene zitsimikize uthenga wa Mneneri Muhammad{s.a.w}).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّاۖ بَل لَّا يَخَافُونَ ٱلۡأٓخِرَةَ
Sichoncho! Koma kuti iwo sakuopa tsiku lachimaliziro.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّآ إِنَّهُۥ تَذۡكِرَةٞ
Sichoncho! Ndithu ichi (Qur’an) ndichikumbutso (chokwanira).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَمَن شَآءَ ذَكَرَهُۥ
Choncho amene wafuna achikumbukire (amene sakufuna ndizake)!
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَا يَذۡكُرُونَ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُۚ هُوَ أَهۡلُ ٱلتَّقۡوَىٰ وَأَهۡلُ ٱلۡمَغۡفِرَةِ
Ndipo sangakumbukire pokhapokha Allah atafuna. Iye ndiye Amene ali woyenera kumuopa, ndiponso ndiye Mwini kukhululukira (amene akumuopa).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
 
แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: Al-Muddaththir
สารบัญสูเราะฮ์ หมายเลข​หน้า​
 
แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - สารบัญ​คำแปล

การแปลความหมายอัลกุรอานเป็นภาษาชิเชวา แปลโดย คอลิด อิบรอฮีม เบตาลา (ed. 2020)

ปิด