Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 伊斯拉仪   段:
وَمَا مَنَعَنَآ أَن نُّرۡسِلَ بِٱلۡأٓيَٰتِ إِلَّآ أَن كَذَّبَ بِهَا ٱلۡأَوَّلُونَۚ وَءَاتَيۡنَا ثَمُودَ ٱلنَّاقَةَ مُبۡصِرَةٗ فَظَلَمُواْ بِهَاۚ وَمَا نُرۡسِلُ بِٱلۡأٓيَٰتِ إِلَّا تَخۡوِيفٗا
Ndipo palibe chimene chikutiletsa kutumiza zizizwa (zomwe akuzipempha) koma kuti anthu akale adazitsutsa. Asamuda tidawapatsa ngamira yaikazi kuti ikhale chizindikiro choonekera (chozizwitsa) koma adaichitira zosayenera; ndipo sititumiza zizizwa ndi cholinga china, koma kuchenjeza.
阿拉伯语经注:
وَإِذۡ قُلۡنَا لَكَ إِنَّ رَبَّكَ أَحَاطَ بِٱلنَّاسِۚ وَمَا جَعَلۡنَا ٱلرُّءۡيَا ٱلَّتِيٓ أَرَيۡنَٰكَ إِلَّا فِتۡنَةٗ لِّلنَّاسِ وَٱلشَّجَرَةَ ٱلۡمَلۡعُونَةَ فِي ٱلۡقُرۡءَانِۚ وَنُخَوِّفُهُمۡ فَمَا يَزِيدُهُمۡ إِلَّا طُغۡيَٰنٗا كَبِيرٗا
Ndipo (kumbuka) pamene tidakuuza kuti ndithu Mbuye wako wawazungulira anthu (mowadziwa bwinobwino;) ndipo sitidawachite maloto omwe tidakuonetsa koma kuti akhale mayeso kwa anthu, (kuti kodi akhulupirira kapena sakhulupirira), ndiponso (kutchula kwa) rntengo wotembeleredwa m’Qur’an (ndimayetseronso kwa iwo;) ndipo tikuwachenjeza, koma (machenjezo athu) sakuwaonjezera china koma kulumpha malire kwakukulu basi.
阿拉伯语经注:
وَإِذۡ قُلۡنَا لِلۡمَلَٰٓئِكَةِ ٱسۡجُدُواْ لِأٓدَمَ فَسَجَدُوٓاْ إِلَّآ إِبۡلِيسَ قَالَ ءَأَسۡجُدُ لِمَنۡ خَلَقۡتَ طِينٗا
Ndipo (akumbutse) pamene tidauza angelo kuti: “Mugwadireni Adam.” Ndipo adamugwadira kupatula Iblis (iye) adati: “Kodi ndimugwadire yemwe mwamlenga ndi dongo?”
阿拉伯语经注:
قَالَ أَرَءَيۡتَكَ هَٰذَا ٱلَّذِي كَرَّمۡتَ عَلَيَّ لَئِنۡ أَخَّرۡتَنِ إِلَىٰ يَوۡمِ ٱلۡقِيَٰمَةِ لَأَحۡتَنِكَنَّ ذُرِّيَّتَهُۥٓ إِلَّا قَلِيلٗا
Adatinso (kwa Allah): “Kodi mukuona uyu amene mwampatsa ulemelero kuposa ine? Ngati mundipatsa nthawi mpaka tsiku la Qiyâma, ndithu ndiononga mbumba yake (yonse) kupatula ochepa basi.”
阿拉伯语经注:
قَالَ ٱذۡهَبۡ فَمَن تَبِعَكَ مِنۡهُمۡ فَإِنَّ جَهَنَّمَ جَزَآؤُكُمۡ جَزَآءٗ مَّوۡفُورٗا
(Allah) adati: “Choka! Amene adzakutsata mwa iwo, ndithu Jahannam ndiyo mphoto yanu mphoto yokwanira.”
阿拉伯语经注:
وَٱسۡتَفۡزِزۡ مَنِ ٱسۡتَطَعۡتَ مِنۡهُم بِصَوۡتِكَ وَأَجۡلِبۡ عَلَيۡهِم بِخَيۡلِكَ وَرَجِلِكَ وَشَارِكۡهُمۡ فِي ٱلۡأَمۡوَٰلِ وَٱلۡأَوۡلَٰدِ وَعِدۡهُمۡۚ وَمَا يَعِدُهُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ إِلَّا غُرُورًا
Ndipo apusitse amene ungawathe mwa iwo ndi liwu lako; ndipo asonkhanitsire gulu lako la nkhondo la okwera akavalo ndi loyenda ndi miyendo; tenga gawo lako pa chuma chawo ndi ana awo; ndipo alonjeze (malonjezo abodza).” Koma satana salonjeza china koma chinyengo basi.
阿拉伯语经注:
إِنَّ عِبَادِي لَيۡسَ لَكَ عَلَيۡهِمۡ سُلۡطَٰنٞۚ وَكَفَىٰ بِرَبِّكَ وَكِيلٗا
“Ndithu akapolo Anga, ulibe nyonga pa iwo.” Ndipo Mbuye wako akukwanira kukhala mtetezi (wawo).
阿拉伯语经注:
رَّبُّكُمُ ٱلَّذِي يُزۡجِي لَكُمُ ٱلۡفُلۡكَ فِي ٱلۡبَحۡرِ لِتَبۡتَغُواْ مِن فَضۡلِهِۦٓۚ إِنَّهُۥ كَانَ بِكُمۡ رَحِيمٗا
Mbuye wanu ndi yemwe amakuyendetserani zombo pa nyanja kuti munke mufunafuna ubwino Wake. Ndithu Iye Ngwachisoni kwa inu.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 伊斯拉仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭